Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • g94 10/8 tsamba 31
  • Mvuu pa Ntchito Yopulumutsa!

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Mvuu pa Ntchito Yopulumutsa!
  • Galamukani!—1994
  • Nkhani Yofanana
  • Tangoonani Chimvuucho!
    Galamukani!—2003
  • Tsaganani Nafe Paulendo Wathu wa Pamtsinje wa Chobe
    Galamukani!—1990
  • M’nkhalango ya Nairobi Zinyama Zimangodziyendera
    Galamukani!—2003
Galamukani!—1994
g94 10/8 tsamba 31

Mvuu pa Ntchito Yopulumutsa!

YOLEMERA kufikira kumatani anayi, mvuu ili nyama yoyamwitsa yachiŵiri mu ukulu pa za pamtunda. Mano ake amphamvuwo angathe kuphwanya bwato mwa kuluma kamodzi kokha. Motero, kagulu kena ka amuna ku Hwange National Park, Zimbabwe, kanadabwa kwambiri pamene kanaona mvuu ikuchita zinthu mumkhalidwe umene unawachititsa chidwi ndi wachilendo​—⁠kunena mosawonjezera mawu.

Amunawo, pamene anali pafupi ndi dziŵe, anaona nswala ziŵiri zikuthamangitsidwa kowopsa ndi mimbulu isanu ndi inayi. Pokhala zosoŵa kothaŵira, nswalazo zinalumphira m’madzi. Mimbuluyo inathamanga m’mbali mwa madzimo, ikumayembekezera pamene nswalazo ziti zitulukire.

Ndiyeno, nswala ina yotopa inayamba kusambira kumka kutsidya lakutali, yosazindikira kuti mimbuluyo inali kuyembekezera kumeneko. Komabe, pamene nswalayo inayandikira kumtunda, amunawo anaona mvuu pafupipo ikumasambira kumka kwa nswalayo. Itaipeza, magazini a African Wildlife akusimba kuti, mvuuyo “inaitembenuza ndi kuikankha bwinobwino kuti isambire kumka kwina.” Nswalayo inamvera. Mvuuyo inatsatira, ikumaikankha panthaŵi ndi nthaŵi pamene nswalayo inafuna kumka kwina.

Pamene nswalayo inafika kolekezera madzi, amunawo anapenyerera mvuuyo ikukankhira nswalayo kutsidya bwinobwino komabe mwamphamvu. Nswalayo inayenda mapazi angapo modzandira, ndiyeno inaima ikumanjenjemera. Posapita nthaŵi, nswalayo inayamba kupita. Mvuuyo inatsatira kufikira nyama ziŵirizo zinazimiririka.

Kodi nchiyani chimene chinachitikira nswala ina ija? Amunawo akusimba kuti mimbuluyo “inamwerekera kwambiri ndi kuonerera kupulumutsako kwakuti nswala inayo inathaŵa mosaonedwa.”

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena