Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • g03 12/8 tsamba 15
  • Sopo ndi “Katemera Amene Mungadzipatse Nokha”

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Sopo ndi “Katemera Amene Mungadzipatse Nokha”
  • Galamukani!—2003
  • Nkhani Yofanana
  • N’chifukwa Chiyani Ukhondo Uli Wofunika?
    Nsanja ya Olonda—2008
  • Njira Zisanu ndi Imodzi Zosamalira Thanzi Lanu
    Galamukani!—2003
  • Akatswiri Ochapa Zovala ku Abidjan
    Galamukani!—2007
  • Njira Zisanu ndi Imodzi Zotetezera Thanzi Lanu
    Galamukani!—1997
Onani Zambiri
Galamukani!—2003
g03 12/8 tsamba 15

Sopo ndi “Katemera Amene Mungadzipatse Nokha”

“MATENDA oopsa kwambiri omwenso ndi achiŵiri pa matenda amene amapha ana m’dzikoli si malungo, chifuwa cha TB, kapena EDZI. Ndi . . . matenda otsegula m’mimba,” inatero magazini ya The Economist. Komabe, ana ambiri mwa ana amene amafa akanatha kukhala ndi moyo pofika lero ngati iwowo ndi mabanja awo akanakhala kuti ankasamba m’manja ndi sopo nthaŵi zonse.

Ochita kafukufuku a pa sukulu ya zaukhondo ya London School of Hygiene and Tropical Medicine anapeza kuti “kusamba bwinobwino m’manja kungachepetse matenda otsegula m’mimba ndi 43 peresenti,” inatero magazini ya The Economist. “Kusamba m’manja kungathandizenso kwambiri kuchepetsa matenda okhudzana ndi kupuma, amene amapha ana kwambiri kuposa matenda ena onse. Kafukufuku amene anachita pa asilikali ambiri a ku America anasonyeza kuti chimfine ndi chifuwa chinachepa ndi 45 peresenti pamene asilikali ankasamba m’manja mwawo kasanu patsiku.” M’mayiko amene akutukuka kumene mabanja ambiri angathe kugula sopo. N’chifukwa chake, moyenerera sopo akutchedwa kuti “katemera amene mungadzipatse nokha.” Ndipo ndi katemera wosapweteka n’komwe!

Baibulo nalonso limalimbikitsa ukhondo. Lemba la 2 Akorinto 7:1 limati: “Tiyeni tidziyeretse, kusiyana nacho chirichonse chimene chikhoza kudetsa thupi ndi mzimu.” (Chipangano Chatsopano Mu Chichewa Cha Lero) Ngakhale kuti Mulungu amaganizira makamaka za kuyera kwathu kwauzimu, amaonanso ukhondo wa thupi lathu kukhala wofunika kwambiri. (Levitiko, machaputala 12 mpaka 15) N’zoona kuti satiyembekezera kuchita zinthu mopambanitsa. Komabe, tiyenera kukhala ndi chizoloŵezi chosamba m’manja mwathu tikachoka ku chimbudzi, tikasambitsa mwana, kapena tikasintha theŵera lake. Tiyeneranso kusamba m’manja tisanayambe kukonza chakudya kapena kudya, ndiponso pa nthaŵi ina iliyonse pamene zingakhale zotheka kufalitsa tizilombo toyambitsa matenda ta majeremusi kapena mavairasi kwa anthu ena. Mwa kusamba m’manja nthaŵi zonse, timasonyeza chikondi chachikristu ku banja lathu ndi onse amene tingakumane nawo.—Marko 12:31.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena