Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • g05 10/8 tsamba 18
  • Nyanja ya Pinki?

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Nyanja ya Pinki?
  • Galamukani!—2005
  • Nkhani Yofanana
  • Baikal Ndi Nyanja Yaikulu Kwambiri Padziko Lonse
    Galamukani!—2007
  • Kodi Nyanja ya Moto N’chiyani? Kodi ndi Yofanana ndi Gehena?
    Kuyankha Mafunso a M’Baibulo
  • Chimene ‘Chizunzo m’Nyanja ya Moto’ Chimatanthauza
    Kodi Moyo Uno Ndiwo Wokha Umene Ulipo?
  • Chuma cha M’nyanja Yaikulu ya ku Central America
    Nsanja ya Olonda—2009
Onani Zambiri
Galamukani!—2005
g05 10/8 tsamba 18

Nyanja ya Pinki?

Yolembedwa ndi wolemba Galamukani! ku Senegal

KODI nyanja ingakhaledi ya pinki? Nyanja ya Retba imatchedwa kuti Nyanja ya Pinki, ndiye popeza kuti ili pa mtunda wa makilomita 30 kuchokera kunyumba kwathu kuno, ku Dakar, Senegal, kumadzulo kwa Africa, taganiza zopita kumeneko kuti tikaone ngati nyanja imeneyi ikuyenera kukhaladi ndi dzina limeneli. Tsopano tafika, tikuona madzi akunyezimira chifukwa cha dzuwa. Kunena zoona, nyanjayi ikuonekadi ya pinki ndipo ndi yokongola kwambiri. Amene akutionetsa malowa akufotokoza kuti dzuwa likawomba pamadziwa, tinthu tinatake tamoyo timene n’tosatheka kutiona ndi maso timasintha mtundu ndiyeno pamenepa m’pamene pamabwerera mtundu wokongolawu. Komabe, kuno kuli zambiri zoti n’kuona osati mtundu wa nyanja wokhawu.

Pansi pa nyanjayi m’malo amene ali osazama kwambiri pali thanthwe la mwala wa mchere. Madzi ake ndi a mchere kwambiri moti munthu umatha kumangoyandama osasambira ndipo alendo ena amapezerapo mwayi woyandama panyanja imeneyi.

Choncho n’zosachita kufunsa kuti Nyanja ya Pinki imeneyi imathandiza anthu ambiri kupeza ndalama. Mwachitsanzo: (1). M’mphepete mwa nyanjayi, muli antchito amene akupakira mchere m’mathiraki. Tayamba taima kaye pang’ono ndipo tikuona mmene anthu akuchotsera mchere m’nyanjayi. Tikuona anthu aimirira m’madzi amene akuwalekeza m’chifuwa, ndipo anthuwa akukumba mchere pogwiritsa ntchito mapiki ataliatali. Akatero akumauika m’mabasiketi n’kukaupakira m’bwato. Mmodzi wa ogwira ntchitowa watiuza kuti, pamatenga maola atatu kuti akumbe mchere wokwana tani imodzi. Mabwato amawadzadza kwambiri moti amayandama pang’onopangono movutikira (2). Mabwatowa akafika kumtunda, azimayi amatsitsa mcherewu n’kuusenza pamutu m’ndowa (3). Amagwira ntchito imeneyi mogwirizana pamodzi ngati mmene amachitira makina aakulu onyamulira katundu.

Ulendo wathuwu unali ulendo wosangalatsa kwambiri. Nyanja ya pinki ndi imodzi mwa zinthu zosangalatsa zomwe zili padziko lathuli lomwe ndi mphatso ya mtengo wapatali yochokera kwa Yehova.—Salmo 115:16.

[Mawu a Chithunzi patsamba 18]

Photo by Jacques CLEMENT, Clichy, FRANCE at http://community.webshots.com/user/pfjc

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena