Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • g 9/07 tsamba 3
  • N’zothetsa Nzeru Ndiponso Zowononga Chikhulupiriro

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • N’zothetsa Nzeru Ndiponso Zowononga Chikhulupiriro
  • Galamukani!—2007
  • Nkhani Yofanana
  • Kodi Baibulo Limanena Zotani pa Nkhani ya Ngozi Zadzidzidzi?
    Kuyankha Mafunso a M’Baibulo
  • Funso Lovuta Kwambiri
    Galamukani!—2006
  • Kodi Mulungu Akutilanga?
    Nsanja ya Olonda—2011
  • N’chifukwa Chiyani Masoka Achilengedwe Achuluka Chonchi?
    Nsanja ya Olonda—2011
Onani Zambiri
Galamukani!—2007
g 9/07 tsamba 3

N’zothetsa Nzeru Ndiponso Zowononga Chikhulupiriro

“MITEMBO inali ngundangunda paliponse, ndipo sitinadziwe n’komwe kuti nyumba yathu inali pati,” anatero bambo wina m’dziko la Sri Lanka, mudzi wawo utafafanizidwa ndi tsunami, mu December 2004. M’nkhani yonena za tsokali, mkonzi wa nkhani zachipembedzo m’nyuzipepala ina, anafotokoza kuti nthawi zina “ndimapemphera nditakwiya kwambiri.”

Anthu ambiri amaganiza kuti masoka achilengedwe ndi chilango chochokera kwa Mulungu. Bambo wina wolemba nkhani za pa Intaneti anafotokoza mphepo yamkuntho imene inachitika m’dera linalake kuti inali “chibakera cha Mulungu.” Ku United States, atsogoleri ena a zipembedzo anafotokoza kuti masoka monga mphepo yamkuntho ya Katrina ndi “mkwiyo wa Mulungu” pa “mizinda yochimwa kwambiri.” Ku Sri Lanka, magulu ena a Abuda olimbikitsa kwambiri chipembedzo chawo ananena kuti Akhristu ndiwo anachititsa tsunami ndipo izi zinangokulitsa kwambiri udani wa pakati pa zipembedzozi. Mkulu wina wa pakachisi wa Ahindu anakhulupirira kuti mulungu wotchedwa Shiva wakwiya chifukwa cha khalidwe loipa la anthu. Ponena za masoka achilengedwe, mtsogoleri wina wa chipembedzo cha Abuda ku United States anati: “Sitikudziwa chifukwa chimene zinthu zimenezi zimachitikira. Ndipo sitikudziwanso chifukwa chimene tinakhalira padziko pano.”

Mukaona zithunzi za nyumba zowonongeka, mitembo ya anthu, ndiponso za anthu othedwa nzeru, kodi nthawi zina mumadzifunsa kuti, ‘N’chifukwa chiyani Mulungu amalola kuti mavuto oterewa azichitika?’ Kapena mumaganiza kuti, ‘Mulungu ayenera kukhala ndi zifukwa zomveka zololera kuti zinthu zimenezi zizichitika koma kungoti sanatidziwitse zifukwazo.’ M’mitu yotsatirayi tikambirana nkhani imeneyi. Tionanso zinthu zomwe anthu angachite popewa kuvulala kwambiri ndiponso kufa kumene ngati zikuoneka kuti masoka achilengedwe atsala pang’ono kuchitika kapenanso ngakhale atachitika.

[Chithunzi patsamba 3]

Atsogoleri ambiri a zipembedzo sadziwa chifukwa chimene Mulungu amalolera kuti pazichitika masoka achilengedwe

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena