Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • g 9/13 tsamba 3
  • Zochitika Padzikoli

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Zochitika Padzikoli
  • Galamukani!—2013
  • Timitu
  • Nkhani Yofanana
  • Arctic
  • Dziko Lonse
  • Britain
  • Democratic Republic of Congo
  • Australia
  • Malo a Zachilengedwe a Belize Barrier Reef—Chuma Chadziko Lonse
    Galamukani!—2007
  • Njovu—Mabwenzi Kapena Adani?
    Galamukani!—1994
  • Kufufuza Njira Yolumikiza Nyanja ya Atlantic ndi Pacific Kumpoto kwa Dziko Lapansi
    Galamukani!—2010
Galamukani!—2013
g 9/13 tsamba 3

ZOCHITIKA PADZIKOLI

Arctic

[Chithunzi patsamba 3]

Pulofesa wina wa payunivesite ya Cambridge, ku Britain, dzina lake Peter Wadhams, ananena kuti: “Zaka 30 zapitazo, madzi ambiri m’dera la Arctic ankakhalabe oundana m’nyengo yotentha poyerekeza ndi masiku ano.” Mu 2012, sitima zapamadzi pafupifupi 50 zinatha kudutsa bwinobwino m’malo amene poyamba sizinkatha kudutsa chifukwa cha madzi oundana. Zimenezi zachitika chifukwa cha kusintha kwa nyengo.

Dziko Lonse

Akatswiri ofufuza apeza kuti mkaka wa m’mawere wa azimayi amene angobereka kumene, umakhala ndi mitundu yosiyanasiyana ya mabakiteliya yoposa 700. Akatswiriwa sankaganiza kuti mabakiteliyawa angakhale ambiri chonchi. Iwo akufufuza kuti adziwe mmene mabakiteliyawa amathandizira kugaya chakudya komanso kuteteza thupi la mwana wongobadwa kumeneyo.

Britain

[Chithunzi patsamba 3]

Pa kafukufuku wina amene asayansi a ku Britain anapanga anapeza kuti, madalayivala amene akudwala chimfine amalephera kuganiza mwachangu poyendetsa galimoto poyerekezera ndi amene akuyendetsa galimoto ataledzera.

Democratic Republic of Congo

[Chithunzi patsamba 3]

Ku Africa, anthu akupha njovu zambiri chaka chilichonse pofuna minyanga yake ndipo anthu akuti zimenezi sizinachitikepo kwina kulikonse. Pa nthawi ina, anthu anachita kukwera helikopita n’kuwombera njovu zambiri pamutu nthawi imodzi.

Australia

[Chithunzi patsamba 3]

Asayansi apeza kuti zinthu zambiri zachilengedwe zopezeka m’madzi pamalo otchedwa Great Barrier Reef zakhala zikufa m’zaka 27 zapitazi. Iwo akuona kuti zimenezi zachitika chifukwa cha kuwomba kwa mphepo ya mkuntho, kubwera kwa nsomba zotchedwa starfish komanso kuwonongeka kwa miyala ya pamalowa chifukwa cha kutentha kwa madzi.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena