Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • g 11/13 tsamba 16
  • Kodi Mumachita “Phwando Nthawi Zonse”?

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Kodi Mumachita “Phwando Nthawi Zonse”?
  • Galamukani!—2013
  • Nkhani Yofanana
  • Muziganiziranso za Mawa
    Nsanja ya Olonda—2007
  • 4 | Muziteteza Chiyembekezo Chanu
    Galamukani!—2022
  • Baibulo Lingakuthandizeni Kukhala Wosangalala
    Nsanja ya Olonda—2005
  • “Wosamalira Chidzudzulo Amachenjera”
    Nsanja ya Olonda—2006
Onani Zambiri
Galamukani!—2013
g 11/13 tsamba 16
[Chithunzi patsamba 16]

Kodi Mumachita “Phwando Nthawi Zonse”?

“Masiku onse a munthu wosautsika amakhala oipa, koma munthu wamtima wosangalala amachita phwando nthawi zonse.”—Miyambo 15:15.

KODI mawu amenewa amatanthauza chiyani? Mawu amenewa akutanthauza mmene munthu amamvera mumtima mwake. “Munthu wosautsika” amangoganizira za zinthu zomwe sizikuyenda bwino zomwe zimachititsa kuti masiku ake akhale “oipa.” Pamene “munthu wamtima wosangalala” amayesetsa kuona zinthu zabwino ndipo zimenezi zimachititsa kuti azisangalala, kapena kuti m’maganizo mwake azikhala ngati ali pa “phwando nthawi zonse.”

Tonsefe timakumana ndi mavuto amene amatilepheretsa kusangalala. Komabe tikhoza kuchita zinthu zina zimene zingatithandize kukhalabe osangalala pamene zinthu sizikutiyendera bwino. Taonani zimene Baibulo limanena.

  • Musamade nkhawa ndi zinthu zomwe sizinachitike. Yesu Khristu anati: “Musamade nkhawa za tsiku lotsatira, chifukwa tsiku lotsatira lidzakhala ndi zodetsa nkhawa zakenso. Zoipa za tsiku lililonse n’zokwanira pa tsikulo.”—Mateyu 6:34.

  • Yesetsani kumaganizira zinthu zimene zikukuyenderani bwino pa moyo wanu. Mukakhumudwa, mungachite bwino kulemba zinthu zonse zimene zikukuyenderani. Muyeneranso kupewa kumangoganizira zimene munalakwitsa kalekale. Muzingoona zimene mwaphunzira pa zimene munalakwitsazo, koma zisamakulepheretseni kuchita zinthu zina. Muzichita ngati dilaivala yemwe amayang’ana pagalasi loonera kumbuyo koma samayang’ana pagalasipo kwa nthawi yaitali. Muzikumbukiranso kuti ‘Mulungu amakhululukadi.’—Salimo 130:4.

  • Mukakhumudwa muzifotokoza mavuto anu kwa munthu amene akhoza kukulimbikitsani. Lemba la Miyambo 12:25 limanena kuti: “Nkhawa” imaweramitsa mtima wa munthu, “koma mawu abwino ndi amene amausangalatsa.” “Mawu abwino” amenewa angachokere kwa munthu wa m’banja mwanu kapena mnzanu. Muyenera kusankha munthu amene samangoganizira za zinthu zimene sizikuyenda bwino koma amene ‘amakukondani nthawi zonse.’—Miyambo 17:17.

Mawu anzeru omwe ali m’Baibulo athandiza anthu ambiri kukhala osangalala ngakhale pamene akukumana ndi mavuto. Tikukhulupirira kuti nanunso mawu amenewa angakuthandizeni.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena