Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • g16 No. 5 tsamba 16
  • “Mfundozi Zindithandiza Kwambiri”

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • “Mfundozi Zindithandiza Kwambiri”
  • Galamukani!—2016
  • Nkhani Yofanana
  • Vidiyo Yatsopano Yothandiza Poyambitsa Maphunziro a Baibulo
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2014
  • Mboni Za Yehova—Gulu la Dzinalo
    Nsanja ya Olonda—1992
  • Kuwonjezera Luso Lathu mu Utumiki—Kugwiritsa Ntchito Mavidiyo Pophunzitsa
    Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Ndandanda ya Misonkhano—2016
  • Anasiya Tsankho
    Galamukani!—2020
Onani Zambiri
Galamukani!—2016
g16 No. 5 tsamba 16
Mphunzitsi wa ku South Korea akuonetsa ana a m’kalasi yake vidiyo ya pa jw.org

“Mfundozi Zindithandiza Kwambiri”

MPHUNZITSI wa pa sukulu ina yasekondale ku South Korea dzina lake Soo-jeong, amagwiritsa ntchito mavidiyo apawebusaiti ya jw.org pophunzitsa. Iye ananena kuti: “Ana a m’kalasi mwanga amasangalala kwambiri akaonera vidiyo yakuti, Kodi Mnzako Weniweni Ungamudziwe Bwanji? Ana ambiri akamaliza kuonera amanena kuti, ‘Sindinaganizirepo mfundo zimenezi ndikamasankha anzanga. Mfundozi zindithandiza kwambiri.’ Ana ena ananena kuti azipita pawebusaitiyi akafuna malangizo pa nkhani zosiyanasiyana.” Soo-jeong ananenanso kuti: “Ndinauzanso aphunzitsi ena za vidiyoyi ndipo akusangalala chifukwa imawathandiza kwambiri akamaphunzitsa.”

Vidiyo inanso imene ana a sukulu ambiri ku South Korea amaona kuti ndi yothandiza ndi yakuti, Kodi Mungatani Kuti Anzanu Asiye Kukuvutitsani? Munthu wina wa m’bungwe lothandiza kupewa zachiwawa pakati pa ana anaonetsapo vidiyoyi kwa ana ena a sukulu. Iye ananena kuti: “Ana ambiri amaikonda vidiyoyi chifukwa cha zithunzi zake zosangalatsa. Imathandizanso ana kudziwa zimene angachite akamavutitsidwa ndiponso mmene angapewere kuvutitsidwa.” Bungweli linapempha chilolezo kuti lizionetsa vidiyoyi kwa ana a m’masukulu osiyanasiyana apulayimale ndipo linaloledwa. Nawonso apolisi akumagwiritsa ntchito mavidiyo apawebusaiti ya jw.org.

Tikukulimbikitsani kuti mupite pawebusaitiyi. Ndi yosavuta kugwiritsa ntchito ndipo mungapange dawunilodi zinthu zongomvetsera, mavidiyo, Mabaibulo ndiponso mabuku ena popanda kulipira chilichonse.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena