Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • g20 No. 2 tsamba 4-5
  • Zimene Ena Amakhulupirira

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Zimene Ena Amakhulupirira
  • Galamukani!—2020
  • Timitu
  • Nkhani Yofanana
  • Ahindu
  • Asilamu
  • Chiphunzitso chachiyuda
  • Abuda
  • Anthu okhulupirira zomwe Confucius ankaphunzitsa
  • Anthu ena okhulupirira zamizimu
  • Akhristu
  • Kodi Baibulo Limanena Zotani?
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yogawira)—2017
  • Funso Lachitatu: N’chifukwa Chiyani Mulungu Amalola Kuti Ndizivutika?
    Nsanja ya Olonda—2012
  • N’chifukwa Chiyani Anthu Akuvutika Chonchi?
    Galamukani!—2011
  • Kodi Tinalengedwa Kuti Tizivutika?
    Galamukani!—2020
Onani Zambiri
Galamukani!—2020
g20 No. 2 tsamba 4-5
Zizindikiro za zipembedzo za Chibuda, Chihindu, anthu okhulupirira za mizimu, Chiyuda, Chikhristu, Chisilamu, komanso anthu okhulupirira zomwe Confucius ankaphunzitsa.

Zimene Ena Amakhulupirira

Ahindu

Chizindikiro cha Chihindu.

amakhulupirira kuti munthu amavutika chifukwa cha zinthu zomwe wachita m’moyo uno, kapena zomwe anachita m’moyo wina m’mbuyomu. Amakhulupiriranso kuti munthu amasiya kuvutika akafika pa nthawi imene imatchedwa kuti moksha, kutanthauza kuti wasiya kubadwanso akafa, chifukwa pa nthawiyi amasiya kuganizira zinthu zosagwirizana ndi zachipembedzo.

Asilamu

Chizindikiro cha Chisilamu.

amakhulupirira kuti mavuto ndi chilango cha machimo a munthu, kapena njira yoyesera chikhulupiriro chake. Dr. Sayyid Syeed, yemwe ndi pulezidenti wa Islamic Society of North America, ananena kuti mavuto amatikumbutsa kuti “nthawi zonse tiziyamikira Mulungu chifukwa cha madalitso omwe amatipatsa komanso kuti tizikumbukira kuthandiza anthu osauka.”

Chiphunzitso chachiyuda

Chizindikiro cha Chiyuda.

chimati munthu aliyense amavutika chifukwa cha zochita zake. Ayuda ena amanena kuti anthu akufa adzauka ndipo kenako anthu abwino omwe anakumana ndi mavuto adzachitiridwa zinthu mwachilungamo. Chiphunzitso china cha Ayuda chotchedwa Kabbalah, chimanena kuti munthu akafa amabadwanso ndipo zimenezi zimapereka mwayi kwa munthuyo woti alape machimo ake.

Abuda

Chizindikiro cha Chibuda.

amakhulupirira kuti munthu akafa amabadwanso ndipo amapitiriza kukumana ndi mavuto osiyanasiyana mpaka pamene adzasiye kuchita, kuganiza, komanso kulakalaka zinthu zoipa. Ndiye akasiya zinthu zimenezi n’kuyamba kuganizira zinthu zabwino, kuchita zinthu zabwino komanso kukhala wodziletsa, amafika pa nthawi yomwe amaitchula kuti nirvana, kutanthauza kuti mavuto ake onse amatheratu.

Anthu okhulupirira zomwe Confucius ankaphunzitsa

Chizindikiro cha anthu okhulupirira zomwe Confucius ankaphunzitsa.

amati mavuto ambiri amachitika chifukwa cha “kulephera komanso zolakwa za anthu.” (A Dictionary of Comparative Religion). Iye ankaphunzitsa kuti ngakhale kuti mavuto akhoza kuchepa ngati munthu atakhala ndi makhalidwe abwino, mavuto ambiri amayambitsidwa ndi “zolengedwa zauzimu zomwe n’zamphamvu kwambiri kuposa anthu. Choncho munthu amangofunika kuvomereza zimene zolengedwa zauzimuzo zasankha.”

Anthu ena okhulupirira zamizimu

Chizindikiro cha anthu okhulupirira za mizimu.

amanena kuti anthu amavutika chifukwa cha zaufiti. Iwo amakhulupirira kuti mfiti zikhoza kubweretsa mwayi kapena tsoka ndipo mavuto omwe mfiti zimayambitsa akhoza kuchepa pochita miyambo yosiyanasiyana. Amakhulupiriranso kuti ngati munthu akudwala chifukwa cholodzedwa, miyambo komanso mankhwala a asing’anga zimathandiza kuti munthuyo achire.

Akhristu

Chizindikiro cha Chikhristu.

amakhulupirira kuti mavuto anayamba chifukwa cha tchimo la anthu awiri oyambirira, monga mmene buku la m’Baibulo la Genesis limafotokozera. Komabe, matchalitchi ambiri awonjezera maganizo awo pa nkhani imeneyi. Mwachitsanzo, Akatolika ena amanena kuti mavuto a munthu akhoza ‘kuperekedwa kwa Mulungu’ ngati pempho kuti Mulunguyo adalitse tchalitchi chawo, kapena agwiritse ntchito mavutowo kuti apulumutse munthu winawake.

KUTI MUDZIWE ZAMBIRI

[Chithunzi patsamba 5]

Onerani vidiyo yakuti Kodi Mulungu Amavomereza Zipembedzo Zonse? pa jw.org.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena