Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • g20 No. 3 tsamba 3
  • Kodi Muli Ndi Mtima Watsankho?

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Kodi Muli Ndi Mtima Watsankho?
  • Galamukani!—2020
  • Nkhani Yofanana
  • Tsankho Likuchitika Padziko Lonse
    Nsanja ya Olonda—2013
  • Kodi Tsankho Lidzatha Liti?
    Nsanja ya Olonda—2013
  • Kodi Ndinu Wochitiridwa Tsankhu?
    Nsanja ya Olonda—1996
  • Zimene Zimayambitsa Tsankho
    Galamukani!—2004
Onani Zambiri
Galamukani!—2020
g20 No. 3 tsamba 3
Anthu awiri akuyenda moyang’anizana. Mmodzi wa anthuwo akuona kuti chithunzithunzi cha mnzakeyo ndi chachikulu kwambiri komanso chooneka moopsa.

Kodi Muli Ndi Mtima Watsankho?

Tsankho lili ngati kachilombo koyambitsa matenda ka vairasi. Mofanana ndi vairasi, anthu amatha kukhala ndi tsankho koma osadziwa. Ndipotu nalonso tsankho limabweretsera munthu mavuto ambiri.

Anthu ena amakhala ndi maganizo atsankho chifukwa chosiyana dziko lochokera, mtundu, fuko kapena chilankhulo. Enanso amakhala ndi maganizo atsankho chifukwa chosiyana chipembedzo, chifukwa chakuti wina ndi mwamuna kapena mkazi, komanso chifukwa chakuti wina ndi wolemera kapena wosauka. Pamene ena amaona anzawo kuti ndi otsika chifukwa cha zaka zimene ali nazo, maphunziro awo, kulumala kapenanso maonekedwe awo. Ngakhale ali ndi maganizo amenewa, iwo amadziona kuti si atsankho.

Kodi n’kutheka kuti nanunso muli ndi maganizo atsankho? Ambiri timatha kudziwa ngati munthu wina ali ndi tsankho. Komatu n’zovuta kudziwa ngati ifeyo tili nalo. Zoona zake n’zakuti m’njira inayake aliyense ndi watsankho. Pulofesa wina wodziwa za chikhalidwe cha anthu, dzina lake David Williams, ananena kuti anthu akakumana ndi munthu wa gulu limene amaliganizira zolakwika, “amachita naye zinthu mosiyana ndi mmene amachitira ndi anthu ena koma sadziwa kuti akutero.”

Mwachitsanzo, ku Balkans kumene Jovica amakhala, kuli anthu a mtundu winawake umene ambiri sagwirizana nawo. Jovica anati: “Ndinkaganiza kuti pakati pa anthu a mtundu umenewo palibepo wabwino. Komatu sindinkaona kuti limeneli ndi tsankho. Ndinkadziuza kuti, ‘chimenechi ndiye chilungamo chake.’”

Maboma ambiri amakhazikitsa malamulo oletsa kusankhana mitundu komanso kuchita zinthu zina zatsankho. Komabe tsankho silikutha. N’chifukwa chiyani zili choncho? N’chifukwa chakuti malamulowo amangonena zimene munthu angachite basi. Malamulowo sangalepheretse munthu kuganizira ena zoipa kapena kumuchotsera mtima woona anthu ena molakwika. Tsankhotu limayambira m’maganizo komanso mumtima mwa munthu. Ndiye kodi tinganene kuti zimene anthu akuchita pofuna kuthetsa tsankho siziphula kanthu? Kodi ilipo njira yothetsera tsankho?

Nkhani zotsatirazi zifotokoza mfundo 5 zomwe zathandiza anthu ambiri kuthetsa tsankho m’maganizo ndi m’mitima yawo.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena