Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • my nkhani 2
  • Munda Wokongola

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Munda Wokongola
  • Bukhu Langa la Nkhani za Baibulo
  • Nkhani Yofanana
  • Mulungu Analenga Kumwamba ndi Dziko Lapansi
    Zimene Tingaphunzire Munkhani za M’Baibulo
  • Amene Anapanga Zinthu Zonse
    Phunzirani kwa Mphunzitsi Waluso
  • Chifukwa Chake Anataya Malo Ao
    Bukhu Langa la Nkhani za Baibulo
  • Uyo Amene Anapanga Zinthu Zonse
    Kumamumvetsera Mphunzitsi Wamkuru’yo
Onani Zambiri
Bukhu Langa la Nkhani za Baibulo
my nkhani 2

NKHANI 2

Munda Wokongola

ONANI pa dziko’pa! N’chokongola chotani nanga m’mene chiri chonse chiriri! Onani udzu ndi mitengo, maluwa n’zinyama zonse. Kodi njobvu ndi mikango ziripo?

Kodi munda wokongola’wu unakhalapo motani? Tiyeni tione.

Mulungu, anayamba wapanga nsipu wokuta dziko. Napanga’nso mitundu yonse ya tomera. Zomera’zi zimakongoletsa dziko. Zimatipatsa’nso zakudya zokoma.

Anapanga’nso nsomba zisambire m’madzi ndi mbalame ziuluke m’mwamba. Anapanga agalu, amphaka ndi akavalo, zinyama zazikulu n’zazing’ono. Kodi n’ziti zimene ziri pafupi ndi nyumba yanu? Kodi sitimakondwera kuti Mulungu anatipangira zonse’zi?

Potsiriza, anapanga mbali ina ikhale malo apadera kwambiri. Anawacha munda wa Edene. Anali abwino’di kotheratu. Chiri chonse chowazungulira chinali chokongola. Mulungu anafuna kuti dziko lonse likhale ngati munda wakongola’wu.

Koma onani’nso chithunzi cha munda’wu. Kodi mukudziwa chimene Mulungu anaona kukhala chikusowamo? Tiyeni tione.

Genesis 1:11-25; 2:8, 9.

Mafunso

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena