Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • my nkhani 12
  • Anthu Amanga Chinsanja

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Anthu Amanga Chinsanja
  • Bukhu Langa la Nkhani za Baibulo
  • Nkhani Yofanana
  • Sanadzipangire Dzina
    Nsanja ya Olonda—1998
  • Nsanja ya ku Babele
    Zimene Tingaphunzire Munkhani za M’Baibulo
  • Kodi Zinenero Zathu Zinayambira pa “Nsanja ya Babele”?
    Nsanja ya Olonda—2013
Bukhu Langa la Nkhani za Baibulo
my nkhani 12

NKHANI 12

Anthu Amanga Chinsanja

ZAKA zambiri zinapitapo. Ana a Nowa anali ndi ana Ochuluka. Ana ao anakula nakhala ndi ana ochuluka. Posapita nthawi panali anthu ochuluka pa dziko lapansi.

Mmodzi wa amene’wa anali chidzukulu cha Nowa chochedwa Nimrode. Iye anali woipa amene anasaka ndi kupha nyama ndi anthu omwe. Nimrode anadzipanga’nso kukhala mfumu kulamulira pa anthu ena. Mulungu sanakonde Nimrode.

Anthu onse pa nthawi’yo analankhula chinenero chimodzi. Nimrode anafuna kuwasonkhanitsa pamodzi kuti adziwalamulira. Chotero kodi mukudziwa chimene anachita? Anauza anthu’wo kumanga mzinda ndi chinsanja. Mukuwaona m’chithunzi’cho akuumba njerwa.

Yehova sanali wokondwa ndi kumanga’ku. Iye anafuna kuti anthu abalalike ndi kukhala pa dziko lonse lapansi. Koma anthu’wo anati: ‘Tiyeni! timange mzinda ndi nsanja yaitali kwambiri yoti nsonga yake idzafike kumwamba. Pompo tidzadzipangira dzina! Anthu’wo anadzifunira ulemu, osati Mulungu.

Chotero Mulungu analetsa anthu’wo kumanga nsanja. Kodi mukudziwa kuti anakuchita motani? Mwa kulankhulitsa anthu zinenero zosiyana mwadzidzidzi. Omanga’wo sanamvane’nso. Ndicho chifukwa chake mzinda’wo unachedwa Ba’bele. kapena Babulo, kutanthauza ”Chisokonezo.”

Anthu’wo tsopano anayamba kubalalika pa Ba’bele. Timagulu timene tinalankhula chinenero chimodzi tinamkera limodzi ku mbali ina ya dziko lapansi.

Genesis 10:1, 8-10; 11:1-9.

Mafunso

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena