Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • my nkhani 20
  • Dina Alowa M’bvuto

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Dina Alowa M’bvuto
  • Bukhu Langa la Nkhani za Baibulo
  • Nkhani Yofanana
  • Muzipewa Kucheza Ndi Anthu a Makhalidwe Oipa
    Nsanja ya Olonda—2011
  • “Thawani Dama”
    Kodi Mungatani Kuti ‘Mulungu Apitirize Kukukondani’?
  • Yakobo ali ndi Banja Lalikulu
    Bukhu Langa la Nkhani za Baibulo
  • Khalani Otetezeka M’gulu la Anthu a Mulungu
    Nsanja ya Olonda—2010
Onani Zambiri
Bukhu Langa la Nkhani za Baibulo
my nkhani 20

NKHANI 20

Dina Alowa M’bvuto

KODI mukuona amene Dina akukacheza nawo? Akumka kukaona atsikana ena okhala m’Kanani. Kodi atate wake akakondwera nazo? Kuti tiyankhe funso’li, tiyeni tikumbukire zimene Abrahamu ndi Isake anaganiza ponena za akazi a m’Kanani.

Kodi Abrahamu anafuna kuti Isake akwatire mtsikana wa M’Kanani? Ai. Kodi Isake ndi Rebeka anafuna kuti mwana wao Yakobo akwatire mtsikana wa m’Kanani? Ai. Kodi mukudziwa chifukwa chake?

N’chifukwa chakuti Akanani analambira milungu yonyenga. Iwo sanali anthu abwino kukwatiwa nawo kapena kuwakwatira, ndipo sanali anthu abwino kuyanjana nawo. Chotero tingakhale otsimikizira kuti Yakobo sakakondwera kuti mwana wake wamkazi anali kupalana ubwenzi ndi atsikana Achikanani’wa.

Ndithudi, Dina analowa m’bvuto. Kodi mukuona mwamuna Wachikanani uyo amene akuyang’ana Dina? Dzina lake ndi Sekemu. Tsiku lina pamene Dina anadza kudzacheza, Sekemu anam’nyenga nam’kakamiza kugona naye. Izi zinali zolakwa, chifukwatu ndiwo amuna ndi akazi okwatirana okha amene ayenera kugona pamodzi. Choipa chochitidwa ndi Sekemu’chi chinachititsa mabvuto ochuluka kwambiri.

Pamene abale a Dina anamva za chochitika’chi, anapsya mtima kwambiri. Awiri a iwo Simeoni ndi Levi, anakwiya kwambiri kwakuti anatenga malupanga nalowa mu mzinda’wo natulukira amuna’wo modzidzimutsa. Iwo ndi abale ao anapha Sekemu ndi amuna ena onse. Yakobo anapsya mtima chifukwa chakuti ana ake anachita choipa’chi.

Kodi bvuto lonse’li linayamba bwanji? N’chifukwa chakuti Dina anapalana ubwezi ndi anthu osamvera malamulo a Mulungu. Sitidzafuna kupanga mabwenzi otero’wo kodi si choncho?

Genesis 34:1-31.

Mafunso

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena