Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • w11 5/1 tsamba 22-23
  • Muzipewa Kucheza Ndi Anthu a Makhalidwe Oipa

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Muzipewa Kucheza Ndi Anthu a Makhalidwe Oipa
  • Nsanja ya Olonda—2011
  • Nkhani Yofanana
  • Kuwonongedwa kwa Sodomu ndi Gomora
    Nsanja ya Olonda—2008
  • Yesu Sanagonje Poyesedwa
    Nsanja ya Olonda—2009
  • Yesu Achiritsa Anthu Mozizwitsa
    Nsanja ya Olonda—2008
  • Yesu Anagometsa Anthu ndi Mawu Ake
    Nsanja ya Olonda—2008
Onani Zambiri
Nsanja ya Olonda—2011
w11 5/1 tsamba 22-23

Zoti Achinyamata Achite

Muzipewa Kucheza Ndi Anthu a Makhalidwe Oipa

Malangizo: Chitani zotsatirazi muli pamalo opanda phokoso. Pamene mukuwerenga mavesiwo, yerekezerani kuti nkhaniyo ikuchitika inuyo muli pomwepo. Yesani kuona m’maganizo mwanu zimene zikuchitika. Mukhale ngati mukumva zimene anthuwo akulankhula. Yesani kumva mmene anthu a m’nkhaniyi akumvera mumtima mwawo.

Amene akutchulidwa kwambiri m’nkhaniyi: Dina, Sekemu, Yakobo, Simiyoni ndi Levi.

Chidule cha Nkhaniyi: Dina anagwiriridwa ndi Sekemu, azichimwene ake anakwiya kwambiri ndi zimenezi ndipo anakonza zokabwezera.

1 ONANI NKHANIYI BWINOBWINO.​—WERENGANI GENESIS 34:1-31.

Kodi mukuganiza kuti Dina ankachita zotani ndi anzake a ku Kanani?

․․․․․

Polankhula ndi Dina, kodi mukuganiza kuti ndi nkhani zotani zomwe Sekemu “ankalankhula naye momunyengerera”?

․․․․․

Kodi mukuganiza kuti Yakobo ankamva bwanji pamene ankakalipira Simiyoni ndi Levi, zomwe zalembedwa m’vesi 30?

․․․․․

2 FUFUZANI MOZAMA.

Kodi mukuganiza kuti n’chifukwa chiyani Dina ankakonda kukacheza ndi ana akazi a Akanani? (Mwachitsanzo, kodi n’kutheka kuti anali ofanana pa zinthu ziti? Kodi ndi zinthu ziti zimene ankazipeza kwa anthu a ku Kanani zomwe mwina kwawo kunalibe?)

․․․․․

Kodi ndi makhalidwe ati a Sekemu amene Dina ayenera kuti ankakopeka nawo? (Werenganinso vesi 3, 12, ndi 19.)

․․․․․

Kodi Baibulo limasonyeza bwanji kuti Dina sanachite kufuna kuti agone ndi Sekemu? (Werenganinso vesi 2.)

․․․․․

Kodi mukuganiza kuti Simiyoni ndi Levi anachita bwino kupha anthu a mumzinda umene Sekemu ankakhala, pobwezera zimene Sekemu anachita? N’chifukwa chiyani mwayankha choncho?

․․․․․

3 GWIRITSANI NTCHITO ZIMENE MWAPHUNZIRA. LEMBANI ZIMENE MWAPHUNZIRA ZOKHUDZA  . . .

Kufunika kosankha mwanzeru anthu ocheza nawo.

․․․․․

Kufunika kodziletsa kuti usabwezere ngakhale utakhala kuti wakwiya pa zifukwa zomveka.

․․․․․

MMENE MUNGAGWIRITSIRE NTCHITO MFUNDOZI.

Kodi mungadziteteze bwanji kuti anthu amene satsatira malamulo a Mulungu asakugwiririreni?

․․․․․

4 M’NKHANIYI, KODI NDI MFUNDO ITI IMENE YAKUKHUDZANI MTIMA KWAMBIRI, NDIPO N’CHIFUKWA CHIYANI?

․․․․․

Ngati mulibe Baibulo, uzani a Mboni za Yehova, kapena kawerengeni Baibulo pa adiresi ya pa Intaneti iyi: www.jw.org.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena