Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • w09 5/1 tsamba 26
  • Yesu Sanagonje Poyesedwa

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Yesu Sanagonje Poyesedwa
  • Nsanja ya Olonda—2009
  • Nkhani Yofanana
  • Kuwonongedwa kwa Sodomu ndi Gomora
    Nsanja ya Olonda—2008
  • Yesu Achiritsa Anthu Mozizwitsa
    Nsanja ya Olonda—2008
  • Yesu Anagometsa Anthu ndi Mawu Ake
    Nsanja ya Olonda—2008
  • Chiwembu Chibwerera Eni Ake
    Nsanja ya Olonda—2008
Onani Zambiri
Nsanja ya Olonda—2009
w09 5/1 tsamba 26

Zoti Achinyamata Achite

Yesu Sanagonje Poyesedwa

Malangizo: Chitani zotsatirazi muli pa malo opanda phokoso. Mukamawerenga mavesiwo, muziyerekezera kuti pamene zinthuzo zinkachitika inuyo munalipo. Yesani kuona nkhanizi m’maganizo mwanu. Yerekezerani kuti mukumva mawu a m’nkhanizi. Yesani kuganizira mmene anthu otchulidwa m’nkhaniyi ankamvera.

ONANI NKHANIYI BWINOBWINO.​—WERENGANI MATEYO 4:1-11.

Kodi mukuganiza kuti chipululu chimene Yesu anakhalako kwa masiku 40 chinali chotani?

․․․․․

Kodi mukuganiza kuti mawu a Satana ankamveka bwanji? Nanga mawu a Yesu?

․․․․․

FUFUZANI MOZAMA.

Kodi Satana anasonyeza bwanji kuti amapezerapo mwayi pa zimene zikum’chitikira munthu? (Werengani vesi 2.)

․․․․․

N’chifukwa chiyani Mdyerekezi sanangouza Yesu kuti amupatsa maufumu onse a padziko lapansi koma, kuti amupatsanso “ulemerero wawo” wonse? (Werengani vesi 8.)

․․․․․

N’chifukwa chiyani Satana anasankha kuyesa Yesu pomuuza kuti amupatsa ulamuliro?

․․․․․

(a) Tikaona mmene Satana anayesera Yesu katatu konse, kodi tinganene kuti Satana ali ndi maganizo otani? ․․․․․

(b) Nanga tinganene kuti Yesu ali ndi maganizo otani tikaona mmene anayankhira Satana pa mayesero onse? ․․․․․

GWIRITSANI NTCHITO ZIMENE MWAPHUNZIRA. LEMBANI ZIMENE MWAPHUNZIRA PONENA ZA . . .

Nthawi imene Satana amakonda kuyesa munthu.

․․․․․

Njira zosiyanasiyana zimene Satana angatiyesere.

․․․․․

Zimene tingachite kuti tisagonje poyesedwa.

․․․․․

M’NKHANIYI, KODI NDI MFUNDO ZITI ZIMENE ZAKUKHUDZANI KWAMBIRI NDIPO N’CHIFUKWA CHIYANI?

․․․․․

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena