Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • w08 5/1 tsamba 23
  • Yesu Achiritsa Anthu Mozizwitsa

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Yesu Achiritsa Anthu Mozizwitsa
  • Nsanja ya Olonda—2008
  • Nkhani Yofanana
  • Kuwonongedwa kwa Sodomu ndi Gomora
    Nsanja ya Olonda—2008
  • Yesu Anagometsa Anthu ndi Mawu Ake
    Nsanja ya Olonda—2008
  • Yesu Sanagonje Poyesedwa
    Nsanja ya Olonda—2009
  • Petulo Akana Yesu
    Nsanja ya Olonda—2008
Onani Zambiri
Nsanja ya Olonda—2008
w08 5/1 tsamba 23

Zoti Achinyamata Achite

Yesu Achiritsa Anthu Mozizwitsa

Malangizo: Chitani zotsatirazi muli pa malo opanda phokoso. Mukamawerenga mavesiwo, muziyerekezera kuti pamene zinthuzo zinkachitika inuyo munalipo. Yesani kuona nkhanizi m’maganizo mwanu. Yerekezerani kuti mukumva mawu a m’nkhanizi.

ONANI BWINOBWINO NKHANI IYI.​—WERENGANI MATEYO 15:21-28.

Kodi mukuganiza kuti mayiyu anamva bwanji mumtima mwake?

․․․․․

Kodi mukuganiza kuti Yesu analankhula motani m’mavesi otsatirawa?

24 ․․․․․ 26 ․․․․․ 28 ․․․․․

FUFUZANI MOZAMA.

Mwa zimene analankhula kapena kuchita, kodi Yesu anasonyeza kangati kuti sanafune kuchiritsa mwana wa mkazi wa mayiyu?

․․․․․

N’chifukwa chiyani poyamba Yesu sanafune kuchiritsa mwanayo?

․․․․․

Nanga n’chifukwa chiyani Yesu anam’chiritsa?

․․․․․

GWIRITSANI NTCHITO ZIMENE MWAPHUNZIRA. LEMBANI ZIMENE MWAPHUNZIRA PONENA ZA . . .

Mmene Yesu anasonyezera kulolera.

․․․․․

Zimene mungachite potsanzira khalidwe limeneli pamene mukuchita zinthu ndi anthu ena.

․․․․․

ONANI BWINOBWINO NKHANI IYI.​—WERENGANI MALIKO 8:22-25.

Kodi mukuganiza kuti m’mudzi ndi kunja kwa mudziwu munali kuoneka zotani ndiponso kumveka phokoso lotani?

․․․․․

FUFUZANI MOZAMA.

Mukuganiza kuti n’chifukwa chiyani Yesu anatengera munthu uja kunja kwa mudzi asanam’chiritse?

․․․․․

GWIRITSANI NTCHITO ZIMENE MWAPHUNZIRA. LEMBANI ZIMENE MWAPHUNZIRA PONENA ZA . . .

Mmene Yesu ankaonera anthu olumala, ngakhale kuti iyeyo analibe chilema chilichonse.

․․․․․

M’NKHANI ZIWIRIZI, KODI NDI MFUNDO ZITI ZIMENE ZAKUKHUDZANI KWAMBIRI NDIPO N’CHIFUKWA CHIYANI?

․․․․․

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena