Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • w08 1/1 tsamba 26
  • Petulo Akana Yesu

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Petulo Akana Yesu
  • Nsanja ya Olonda—2008
  • Nkhani Yofanana
  • Kuwonongedwa kwa Sodomu ndi Gomora
    Nsanja ya Olonda—2008
  • Yesu Achiritsa Anthu Mozizwitsa
    Nsanja ya Olonda—2008
  • Yesu Anagometsa Anthu ndi Mawu Ake
    Nsanja ya Olonda—2008
  • Yesu Sanagonje Poyesedwa
    Nsanja ya Olonda—2009
Onani Zambiri
Nsanja ya Olonda—2008
w08 1/1 tsamba 26

Zoti Achinyamata Achite

Petulo Akana Yesu

Malangizo: Powerenga Baibulo khalani pa malo abata. Pamene mukuwerenga malemba, yerekezerani kuti inuyo mulipo pamene zimene mukuwerengazo zikuchitika. Onani zochitikazo m’maganizo mwanu. Yerekezerani kuti mukumva zimene anthuwo akulankhula. Yerekezerani kuti mukumva monga mmene anthu a m’nkhaniyo akumvera.

FOTOKOZANI MWACHIDULE.​—WERENGANI MATEYO 26:31-35, 69-75.

Kodi mukuganiza kuti m’nkhaniyi munali anthu angati?

․․․․․

Kodi mukuganiza kuti anthu amene analankhula ndi Petulo anali aubwenzi? ofunitsitsa kudziwa? okwiya? zina?

․․․․․

Kodi mukuganiza kuti Petulo anamva bwanji ndi zimene anthuwo ankanena?

․․․․․

N’chifukwa chiyani Petulo anakana Yesu? Kodi n’chifukwa choti analibe chikondi, kapena pali chifukwa china?

․․․․․

SINKHASINKHANI KWAMBIRI.​—WERENGANI LUKA 22:31-34; MATEYO 26:55-58; YOHANE 21:9-17.

Kodi kudzidalira mopambanitsa kunachititsa bwanji kuti Petulo alakwe?

․․․․․

Kodi Yesu anasonyeza bwanji kuti ankakhulupirira Petulo, ngakhale kuti iye ankadziwa kuti Petuloyo amukana?

․․․․․

Ngakhale kuti Petulo anakana Yesu, kodi iye anasonyeza motani chikhulupiriro cholimba kuposa ophunzira ena?

․․․․․

Kodi Yesu anasonyeza bwanji kuti anakhululukira Petulo?

․․․․․

Kodi mukuganiza kuti n’chifukwa chiyani Yesu anafunsa Petulo katatu kuti: “Kodi umandikonda ine?”

․․․․․

Kodi mukuganiza kuti Petulo anamva bwanji atatha kukambirana zimenezi ndi Yesu, ndipo n’chifukwa chiyani mukuganiza choncho?

․․․․․

GWIRITSANI NTCHITO ZIMENE MWAPHUNZIRA. LEMBANI ZIMENE MWAPHUNZIRA ZOKHUDZA . . .

Kuopa anthu.

․․․․․

Mmene Yesu anasonyezera chifundo kwa ophunzira ake, ngakhale pamene ophunzirawo analakwa.

․․․․․

Kodi n’chiyani chimene chakusangalatsani kwambiri mu nkhaniyi, ndipo n’chifukwa chiyani?

․․․․․

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena