Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • w08 9/1 tsamba 24
  • Yesu Anagometsa Anthu ndi Mawu Ake

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Yesu Anagometsa Anthu ndi Mawu Ake
  • Nsanja ya Olonda—2008
  • Nkhani Yofanana
  • Kuwonongedwa kwa Sodomu ndi Gomora
    Nsanja ya Olonda—2008
  • Yesu Achiritsa Anthu Mozizwitsa
    Nsanja ya Olonda—2008
  • Yesu Sanagonje Poyesedwa
    Nsanja ya Olonda—2009
  • Petulo Akana Yesu
    Nsanja ya Olonda—2008
Onani Zambiri
Nsanja ya Olonda—2008
w08 9/1 tsamba 24

Zoti Achinyamata Achite

Yesu Anagometsa Anthu ndi Mawu Ake

Malangizo: Chitani zotsatirazi muli pa malo opanda phokoso. Mukamawerenga mavesiwo, muziyerekezera kuti pamene zinthuzo zinkachitika inuyo munalipo. Yesani kuona nkhaniyi m’maganizo mwanu. Yerekezerani kuti mukumva mawu a m’nkhaniyi. Yesetsani kumva mu mtima mwanu ngati mmene ankamvera anthu a m’nkhaniyi.

ONANI BWINOBWINO NKHANIYI.​—WERENGANI LUKA 2:41-47.

Kodi mukawerenga vesi 46 mukuganiza kuti Yesu ankakambirana zinthu zotani ndi aphunzitsi?

․․․․․

FUFUZANI MOZAMA.

Kodi mukuganiza kuti n’chifukwa chiyani Yesu anatha kukambirana ndi atsogoleri a chipembedzo adakali wamng’ono? Kodi n’chifukwa choti anali wangwiro basi, kapena panalinso zifukwa zina?

․․․․․

ONANI BWINOBWINO NKHANIYI.​—WERENGANI LUKA 2:48-52.

Kodi mukuganiza kuti nkhope ya Yesu inkaoneka bwanji pamene ananena mawu akuti: “Mumandifunafuna chifukwa chiyani?”

․․․․․

N’chifukwa chiyani tinganene motsimikiza kuti polankhula ndi makolo ake, Yesu sanalankhule mwaukali kapena mopanda ulemu?

․․․․․

FUFUZANI MOZAMA.

N’chifukwa chiyani n’zosadabwitsa kuti Yosefe ndi Mariya anazunzika mumtima Yesu atasowa?

․․․․․

Ngakhale kuti Yesu anali wangwiro, n’chifukwa chiyani iye anafunikirabe kupitiriza kumvera makolo ake?

․․․․․

Kodi mukuganiza kuti Yesu anachita manyazi chifukwa choti anadzudzulidwa pamaso pa anthu amene anagoma naye?

․․․․․

GWIRITSANI NTCHITO ZIMENE MWAPHUNZIRA. LEMBANI ZIMENE MWAPHUNZIRA PONENA ZA . . .

Kugonjera.

․․․․․

Ubwino wa kuphunzira Baibulo munthu adakali wamng’ono.

․․․․․

M’NKHANIYI, KODI NDI MFUNDO ZITI ZIMENE ZAKUKHUDZANI KWAMBIRI NDIPO N’CHIFUKWA CHIYANI?

․․․․․

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena