Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • my nkhani 45
  • Kuoloka Mtsinje wa Yordano

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Kuoloka Mtsinje wa Yordano
  • Bukhu Langa la Nkhani za Baibulo
  • Nkhani Yofanana
  • Yehova Anasankha Yoswa
    Zimene Tingaphunzire Munkhani za M’Baibulo
  • Kodi Likasa la Pangano N’chiyani?
    Kuyankha Mafunso a M’Baibulo
  • Mfundo Zazikulu za M’buku la Yoswa
    Nsanja ya Olonda—2004
  • Chigumula Chachikulu
    Bukhu Langa la Nkhani za Baibulo
Onani Zambiri
Bukhu Langa la Nkhani za Baibulo
my nkhani 45

NKHANI 45

Kuoloka Mtsinje wa Yordano

TAONANI! Aisrayeli akuoloka Mtsinje wa Yordano! Koma kodi madzi ali kuti? Chifukwa mvula yochuluka imabvumba nthawi imene’yo ya chaka, mtsinje’wo unali wodzadza kwambiri mphindi zowerengeka zapita’zo. Koma tsopano madzi onse apita! Ndipo Aisrayeli akuoloka pouma monga momwe anachitira’di pa Nyanja Yofiira! Kodi madzi onse anamka kuti? Tiyeni tione.

Pamene inafika nthawi yoti Aisrayeli aoloke Mtsinje wa Yordano, nazi zimene Yehova anauza Yoswa kuuza anthu: ‘Ansembe ayenera kusenza likasa la chipangano ndi kutsogolera ife. Pamene iwo athibika mapazi ao m’madzi a Mtsinje wa Yordano, pamenepo madzi’wo adzaleka kuyenda.’

Chotero ansembe akusenza likasa la chipangano, nayenda nalo patsogolo pa anthu. Pofika ku Yordano, ansembe’wo akulowa m’madzimo. Iwo akuthamanga kwambiri ndipo ngwozama. Koma pamene mapazi ao angokhudza madzi’wo, akuyamba kuleka kuyenda! N’chozizwitsa! Yehova wasonkhanitsa pamodzi madzi kumtunda’ko. Chotero, posapita nthawi mulibe’nso madzi mu mutsinje’wo!

Ansembe onyamula likasa’wo akumka pakati pa mtsinje wouma’wo. Kodi mukuwaona m’chithunzi’cho? Ataima pamenepo, Aisrayeli onse akuyenda kuoloka Mtsinje wa Yordano pouma!

Ali yense ataoloka, Yehova akuuza Yoswa kuuza amuna amphamvu 12 kuti: ‘Lowani mu mtsinje kumene kwaima ansembe onyamula likasa’wo. Tolani miyala 12, ndi kuiimika pamene inu nonse mudzagona. Ndiyeno, m’tsogolo, akakufunsani ana anu chimene miyala’yi imatanthauza, muziwauza kuti madzi anaima pamene likasa la Yehova linaoloka Yordano. Miyala’yi idzakukumbutsani za chozizwitsa’chi!’ Yoswa akuimika’nso miyala 12 pamene panaima ansembe m’mbali mwa mtsinje’wo.

Pomaliza Yoswa akuuza ansembe osenza likasa kuti: ‘Tulukani m’Yordano.’ Atangotuluka, mtsinje’wo ukuyamba’nso kuyenda.

Yoswa 3:1-17; 4:1-18.

Mafunso

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena