Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • my nkhani 46
  • Malinga a Yeriko

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Malinga a Yeriko
  • Bukhu Langa la Nkhani za Baibulo
  • Nkhani Yofanana
  • Rahabi Anabisa Aisiraeli Okafufuza Dziko
    Zimene Tingaphunzire Munkhani za M’Baibulo
  • Rahabi Abisa Azondi
    Bukhu Langa la Nkhani za Baibulo
  • Rahabi Ankakhulupirira Yehova
    Phunzitsani Ana Anu
  • ‘Anaonedwa Ngati Wolungama Chifukwa cha Ntchito Zake’
    Nsanja ya Olonda—2013
Onani Zambiri
Bukhu Langa la Nkhani za Baibulo
my nkhani 46

NKHANI 46

Malinga a Yeriko

KODI n’chiani chimene chikugwetsa malinga a Yeriko’wa? Kukuonekera ngati kuti pagwera bomba lalikulu. Koma m’masiku’wo kunalibe mabomba; iwo analibe ngakhale mfuti. N’chozizwitsa china cha Yehova! Tiyeni tiphunzire m’mene zinachitikira.

Imvani zimene Yehova akuuza Yoswa: ‘Iwe ndi ankhondo ako muzizungulira mzinda’wo. Muuzungulire kamodzi pa tsiku kwa masiku asanu ndi limodzi. Mumke ndi likasa la chipangano lomwe. Ansembe asanu ndi awiri ayenera kulitsogolera ndi kuomba mphalasa zao.

‘Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri muzungulira mzinda nthawi zisanu ndi ziwiri. Ndiyeno n’kuliza chilizire mphalasa’zo, n’kuuza ali yense kufuulitsa. Ndipo malinga’wo adzagwa pansi phwata!’

Yoswa ndi anthu’wo akuchita zonena za Yehova. Pozungulira, ali yense ali chete. Palibe wolankhula liu. Zokha zimene zikumveka ndizo mphalasa ndi mlikiti wa mapazi. Adani a anthu a Mulungu m’Yerikomo ayenera kukhala akuchita mantha. Kodi mukuona chingwe chofiira chikulendewera pa zenera’cho? Kodi n’zenera la yani iro? Inde, Rahabi wachita zimene azondi aja anamuuza. A m’banja mwake onse ali m’katimo akuonera naye.

Kenako, pa tsiku lachisanu ndi chiwiri, atazungulira kasanu ndi kawiri, mphalasa zikulizidwa, ankhondo’wo akupfuula, ndipo malinga akugwa. Yoswa akulamulano kuti: ‘Iphani ali yense mu mzinda’wo. Tenthani chiri chonse. Sungani kokha siliva, golidi, mkuwa ndi chitsulo, n’kuzipereka zilowe mosungira mwa chihema cha Yehova.’

Yoswa akuuza azondi awiri’wo, kuti: ‘Lowani m’nyumba ya Rahabi, nimum’tulutse iye ndi a m’banja lake onse.’ Rahabi ndi a m’banja lake apulumitsidwa, monga momwe analonjezera azondi’wo.

Yoswa 6:1-25.

Mafunso

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena