Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • my nkhani 86
  • Amuna Atsogozedwa ndi Nyenyezi

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Amuna Atsogozedwa ndi Nyenyezi
  • Bukhu Langa la Nkhani za Baibulo
  • Nkhani Yofanana
  • Yehova Anateteza Yesu
    Zimene Tingaphunzire Munkhani za M’Baibulo
  • Yesu ndi Openda Nyenyezi
    Munthu Wamkulu Woposa Onse Amene Anakhalako
  • Kodi Nyenyezi Imene Inatsogolera “Anzeru a Kum’mawa” Inali Yotani?
    Galamukani!—2009
  • Okhulupirira Nyenyezi Anapita Kukaona Yesu
    Yesu—Ndi Njira, Choonadi ndi Moyo
Onani Zambiri
Bukhu Langa la Nkhani za Baibulo
my nkhani 86

NKHANI 86

Amuna Atsogozedwa ndi Nyenyezi

KODI mukuona nyenyezi yowala’yo imene amuna’wa akuiloza? Pamene ananyamuka m’Yerusalemu, nyenyezi’yo inaoneka. Amuna’wa ngochokera Kum’mawa, ndipo iwo amaphunzira nyenyezi. Iwo amakhulupirira kuti nyenyezi yatsopano’yi ikuwatsogolera kwa wina wake wofunika.

Pamene amuna’wo akufika ku Yerusalemu, iwo anafunsa kuti: ‘Kodi ali kuti mwana amene adzakhala mfumu ya Ayuda?’ “Ayuda” ndi dzina lina la Aisrayeli. ‘Tinayamba kuona nyenyezi ya mwana’yo tikali Kum’mawa,’ anatero amuna’wo, ndipo tadza kudzam’lambira.’

Herode, amene ali mfumu pa Yerusalemu, pomva izi, anabvutika maganizo. Iye sanafune kuti mfumu ina itenge malo ake. Chotero iye anaitana akulu ansembe nawafunse kuti: ‘Kodi mfumu yolonjezedwa’yo idzabadwira kuti’ Iwo akuyankha kuti: ‘Baibulo limati m’Betelehemu.’

Chotero Herode anaitana amuna Akum’mawa’wo, nati nawo: ‘Mukani mukafune-fune kamwana’ko. Mutakapeza, zandidziwitseni. Nane’nso ndikufuna kumka kukakalambira.’ Koma, kweni-kweni, Herode anafuna kupeza mwana’yo ndi kum’pha!

Ndiyeno nyenyezi’yo ikuyenda patsogolo pa amuna’wo kumka ku Betelehemu, ndipo ikuima pa malo pamene pali mwana’yo. Atalowa m’nyumbamo amuna’wo, akupezamo Mariya ndi mwana’yo Yesu. Iwo akutulutsa mphatso nazipereka kwa Yesu. Koma kenako Yehova akuwachenjeza m’kulota kusabwerera kwa Herode. Chotero akubwerera kwao pa njira ina.

Herode atamva kuti amuna a Kum’mawa aja abwerera kwao, akupsya mtima kwambiri. Chotero akulamula kuti ana amuna onse m’Betelehemu a zaka ziwiri ndi zocheperapo aphedwe. Koma Yehova akuchenjeza Yosefe pasadakhale m’kulota, ndipo Yosefe ndi banja lake akuchoka kumka ku Betelehemu. Kenako, Yosefe atamva kuti Herode wafa, akutenga Mariya ndi Yesu nabwerera ku Nazarete kwao. Kuno ndiko kumene Yesu anakulira.

Kodi muganiza kuti ndani amene anapangitsa nyenyezi yatsopano’yo kuwala? Pajatu, choyamba amuna’wo anamka ku Yerusalemu ataona nyenyezi’yo. Satana Mdierekezi anafuna kupha Mwana wa Mulungu, ndipo anadziwa kuti Mfumu Herode ya Yerusalemu ikayesa kum’pha. Chotero Satana ndiye amene ayenera kukhala atapangitsa nyenyezi’yo kuwala.

Mateyu 2:1-23; Mika 5:2.

Mafunso

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena