Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • my nkhani 87
  • Mnyamata Yesu m’Kachisi

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Mnyamata Yesu m’Kachisi
  • Bukhu Langa la Nkhani za Baibulo
  • Nkhani Yofanana
  • Zimene Yesu Anachita Ali Wamng’ono
    Zimene Tingaphunzire Munkhani za M’Baibulo
  • Yosefe ndi Banja Lake Anapita ku Yerusalemu
    Yesu—Ndi Njira, Choonadi ndi Moyo
  • Yesu Anaphunzira Kumvera
    Nsanja ya Olonda—2010
  • Mafunso Ochokera kwa Owerenga
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2023
Onani Zambiri
Bukhu Langa la Nkhani za Baibulo
my nkhani 87

NKHANI 87

Mnyamata Yesu m’Kachisi

TAONANI kamnyamata’ko kakulankhula ndi anthu achikulire’wa. Iwo ndi aphunzitsi m’kachisi wa Mulungu pa Yerusalemu. Kamnyamata’ko ndiko Yesu. Iye wasinkhukirapo. Tsopano ali ndi zaka 12.

Aphunzitsi’wo akudabwa kwambiri kuti iye akudziwa zambiri zonena za Mulungu ndi zolembedwa m’Baibulo. Koma n’chifukwa ninji Yosefe ndi Mariya nawo’nso salipo? Kodi ali kuti? Tiyeni tione.

Chaka chiri chonse Yosefe anali kumka ndi banja lake ku Yerusalemu kaamba ka phwando lapadera la Paskha. Ndi ulendo wautali kuchokera ku Nazarete kukafika ku Yerusalemu Palibe anali ndi galimoto, ndipo palibe matreni. Analibe pa nthawi’yo. Ochuluka anayenda pansi, ndipo kumawatengera masiku atatu kukafika ku Yerusalemu.

Pa nthawi ino Yosefe anali ndi banja lalikulu. Chotero pali ang’ono ndi alongo a Yesu owayang’anira. Eya, chaka chino Yosefe ndi Mariya anali atanyamuka ndi ana ao pa ulendo wao wautali’wo wobwerera ku Nazarete. Iwo akuganiza kuti Yesu akuyendera limodzi ndi oyenda ena’wo. Koma pamene akuima pa mapeto a tsiku, Yesu palibe. Iwo akum’funa-funa pakati pa achibale ao ndi mabwenzi, koma sali nawo! Chotero akubwerera ku Yerusalemu kukam’funa-funa.

Potsiriza iwo akum’peza pano ndi aphunzitsi. Iye akuwamvetsera nawafunsa mafunso. Ndipo anthu onse akudabwa ndi nzeru za Yesu. Koma Mariya akuti: ‘Mwanawe, watichitiranji izi? Atate wako ndi ine takhala odera nkhawa kwambiri kuyesa-yesa kukupeza.’

‘Mumandifuniranji?’ akutero Yesu. ‘Kodi simunadziwe kuti ndiyenera kukhala m’nyumba ya Atate wanga?’

Inde, Yesu amakonda kukhala kumene iye angaphunzire za Mulungu. Kodi m’menemo sindimo m’mene ife’nso tiyenera kumvera? Kwaoko ku Nazarete, Yesu ankapita ku misonkhano ya kulambira mlungu ndi mlungu. Chifukwa nthawi zonse anamvetsera, anaphunzira zinthu zambiri za m’Babulo. Tiyeni tikhale ngati Yesu ndi kutsatira chitsanzo chake.

Luka 2:41-52; Mateyu 13:53-56.

Mafunso

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena