Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • my nkhani 98
  • Pa Phiri la Azitona

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Pa Phiri la Azitona
  • Bukhu Langa la Nkhani za Baibulo
  • Nkhani Yofanana
  • Yesu Anabwerera Kumwamba
    Zimene Tingaphunzire Munkhani za M’Baibulo
  • Kukumbukira Masiku Omaliza a Yesu Padziko
    Nsanja ya Olonda—1998
  • “Yafika Nthaŵi”!
    Nsanja ya Olonda—2000
  • Yesu Abwerera Kumwamba
    Bukhu Langa la Nkhani za Baibulo
Onani Zambiri
Bukhu Langa la Nkhani za Baibulo
my nkhani 98

NKHANI 98

Pa Phiri la Azitona

UYU ndi Yesu pa Phiri la Azitona. Amuna anai ali naye’wo ndiwo atumwi ake. Iwo ndi abale Andreya ndi Petro, ndipo’nso abale’wo Yakobo ndi Yohane. Uyo mukumuona cha uko’yo ndi kachisi wa Mulungu mu Yerusalemu.

Papita masiku awiri chiyambire pamene anakwera bulu kulowa mu Yerusalemu. N’Lachiwiri. M’mawa wa tsiku’lo Yesu anali pa kachisi. Pamenepo ansembe anayesa kugwira Yesu kuti amuphe. Koma iwo anali kuopa kuchita izi chifukwa anthu anakonda Yesu.

‘Njoka inu ndi ana a njoka!’ anawatero Yesu atsogoleri achipembedzo. Ndiyeno iye anati Mulungu akawalanga chifukwa cha zoipa zonse zimene iwo anachita. Pambuyo pake Yesu anadza ku Phiri la Azitona, ndipo atumwi anai’wa anayamba kufunsa mafunso. Kodi mukudziwa zimene iwo akufunsa Yesu?

Atumwi’wo akufunsa zinthu zina za m’tsogolo. Iwo akudziwa kuti Yesu adzathetsa kuipa konse pa dziko lapansi. Koma iwo akufuna kudziwa nthawi imene zimene’zi zidzachitika. Kodi ndi liti pamene Yesu adzadza kudzalamulira monga Mfumu?

Yesu akudziwa kuti otsatira ake pa dziko lapansi sadzakhala okhoza kumuona’nso. Izi ziri chifukwa chakuti iye adzakhala ali kumwamba, ndipo iwo sadzakhoza kumuona kumene’ko. Chotero Yesu akuuza atumwi ake zina za zinthu zimene zidzakhala zikuchitika pa dziko lapansi pamene iye akulamulira monga Mfumu kumwamba. Kodi ndi ziti zimene ziri zina za zinthu zimene’zi?

Yesu akunena kuti kudzakhala nkhondo zazikulu, anthu ambiri adzakhala akudwala, ndi anjala, upandu udzakhala woipa kwambiri, ndipo padzakhala zibvomezi zazikulu. Yesu ananena’nso kuti mbiri yabwino yonena za ufumu wa Mulungu idzalalikidwa kuli konse pa dziko lapansi. Kodi taona zinthu’zi zikuchitika m’nthawi yathu? Inde! Ndipo chotero tingathe kukhala otsimikizira kuti Yesu tsopano akulamulira kumwamba. Posachedwa iye adzathetsa kuipa konse pa dziko lapansi.

Mateyu 21:46; 23:1-39; 24:1-14; Marko 13:3-10.

Mafunso

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena