Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • my nkhani 114
  • Mapeto a Kuipa Konse

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Mapeto a Kuipa Konse
  • Bukhu Langa la Nkhani za Baibulo
  • Nkhani Yofanana
  • Nyama Zokongola Mogometsa
    Galamukani!—2011
  • Paradaiso Watsopano pa Dziko
    Bukhu Langa la Nkhani za Baibulo
  • Nkhondo ya Mulungu Idzathetsa Nkhondo Zonse
    Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Ndandanda ya Misonkhano—2019
  • Zimene Baibulo Limaneneratu Zimakwaniritsidwa
    Bukhu Langa la Nkhani za Baibulo
Bukhu Langa la Nkhani za Baibulo
my nkhani 114

NKHANI 114

Mapeto a Kuipa Konse

KODI mukuonanji pano? Inde, gulu la nkhondo lokwera pa akavalo oyera. Koma onani kumene iwo akuchokera. Akavalo’wo akuthamanga kuchokera kumwamba m’mitambo! Kodi kumwamba kuli akavalo eni-eni?

Ai, awa si akavalo eni-eni. Tikudziwa izi chifukwa chakuti akavalo sangathamange m’mitambo. Kodi si choncho? Koma Baibulo limanena za akavalo a kumwamba. Kodi mukudziwa chifukwa chake limatero?

N’chifukwa chakuti pa nthawi ina akavalo anagwiritsiridwa ntchito m’kumenya nkhondo. Chotero Baibulo limasimba za anthu kukhala akukwera pa akavalo akutsika kuchokera kumwamba kusonyeza kuti Mulungu ali ndi nkhondo yoti amenyane ndi anthu pa dziko lapansi. Kodi mukudziwa chimene malo a nkhondo’yi akuchedwa? Armagedo. Nkhondo imene’yo iyenera kuthetsa kuipa konse pa dziko lapansi.

Yesu ndiye adzatsogolera m’kumenya nkhondo’yi pa Armagedo. Pajatu, Yesu ndiye amene Yehova anam’sankha kukhala mfumu ya boma Lake. Ndicho chifukwa chake Yesu wabvala chisoti chachifumu. Ndipo lupanga’lo limasonyeza kuti iye adzapha adani a Mulungu onse. Kodi tiyenera kudabwitsidwa kuti Mulungu adaononga anthu onse.

Bwererani ku Nkhani 10. Kodi mukuonapo chiani? Inde, Chigumula chachikulu chimene chinaononga anthu oipa. Kodi ndani amene anachititsa Chigumula chimene’cho. Yehova Mulungu. Tsopano onani Nkhani 15. Kodi n’chiani chimene chikuchitika pano? Sodomu ndi Gomora akuonongedwa ndi moto umene Yehova akutumiza.

Tembenukirani ku Nkhani 33. Onani chimene chikuchitikira akavalo ankhondo’wo ndi magaleta a Aigupto. Kodi ndani amene anachititsa madzi’wo kuwaphimba. Yehova. Iye anakuchita kutetezera anthu ake. Onani Nkhani 76. Mudzaonamo kuti Yehova analola’di anthu ake Aisrayeli, kuonongedwa chifukwa cha kuipa kwao.

Tsono, sitiyenera kudabwa kuti Yehova adzatumiza magulu ake ankhondo kudzathetsa kuipa konse pa dziko lapansi. Koma taganizirani chimene zimene’zo zidzatanthauza! Tembenukirani kutseri’ku tione.

Chibvumbulutso 16:16; 19:11-16.

Mafunso

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena