Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • gf phunziro 8 tsamba 14
  • Kodi Adani a Mulungu Ndani?

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Kodi Adani a Mulungu Ndani?
  • Mungathe Kukhala Bwenzi la Mulungu!
  • Nkhani Yofanana
  • Khalani Maso Satana Akufuna Kukumezani
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova—2015
  • Kodi Mumamudziwa Bwino Mdani Wanu?
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2018
  • Satana
    Galamukani!—2013
  • Kodi Mdyerekezi Ndani?
    Kodi Mulungu Amafunanji kwa Ife?
Onani Zambiri
Mungathe Kukhala Bwenzi la Mulungu!
gf phunziro 8 tsamba 14

PHUNZIRO 8

Kodi Adani a Mulungu Ndani?

Mdani wamkulu wa Mulungu ndi Satana Mdyerekezi. Iye ndi cholengedwa chauzimu chimene chinapandukira Yehova. Satana akupitirizabe kulimbana ndi Mulungu ndi kuchititsa mavuto aakulu kwa anthu. Satana ndi woipa. Iye ndi wabodza ndi wambanda.—Yohane 8:44.

Ziwanda

Zolengedwa zinanso zauzimu zinagwirizana ndi Satana pa kupandukira kwake Mulungu. Baibulo limazitcha ziŵanda. Monga Satana, ziŵandanso ndi adani a anthu. Zimakonda kuvulaza anthu. (Mateyu 9:32, 33; 12:22) Yehova adzawononga Satana limodzi ndi ziŵanda zake kwamuyaya. Iwo atsala ndi nthaŵi yochepa kwambiri yopitiriza kuvutitsa anthu.—Chivumbulutso 12:12.

Ngati mukufuna kukhala bwenzi la Mulungu, musachite zimene Satana amafuna kuti muchite. Satana ndi ziŵandazo amadana ndi Yehova. Iwo ndi adani a Mulungu, ndipo amafuna kukuchititsani kukhalanso mdani wa Mulungu. Muyenera kusankha amene mukufuna kum’kondweretsa—Satana kapena Yehova. Ngati mukufuna moyo wosatha, sankhani kuchita chifuniro cha Mulungu. Satana ali ndi machenjera ambiri ndi njira zimene amanyenga nazo anthu. Anthu ambiri akupusitsidwa naye.—Chivumbulutso 12:9.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena