Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • be phunziro 4 tsamba 93-tsamba 96 ndime 2
  • Kulankhula Mosadodoma

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Kulankhula Mosadodoma
  • Pindulani ndi Sukulu ya Utumiki wa Mulungu
  • Nkhani Yofanana
  • Kulankhula Nkhani Mosadodoma, Mokambirana Komanso Motchula Bwino Mawu
    Buku Lolangiza la Sukulu ya Utumiki Wateokalase
  • Kodi Mungatani Kuti Muchepetse Vuto Lochita Chibwibwi?
    Galamukani!—2010
  • Kukhala ndi Kalankhulidwe Kabwino Tsiku ndi Tsiku
    Buku Lolangiza la Sukulu ya Utumiki Wateokalase
  • ‘Chitani Khama Kuŵerenga Poyera’
    Buku Lolangiza la Sukulu ya Utumiki Wateokalase
Onani Zambiri
Pindulani ndi Sukulu ya Utumiki wa Mulungu
be phunziro 4 tsamba 93-tsamba 96 ndime 2

PHUNZIRO 4

Kulankhula Mosadodoma

Kodi muyenera kuchita motani?

Ŵerengani ndi kulankhula m’njira yakuti mawu ndi malingaliro anu azimveka bwinobwino. Pamene mulankhula mosadodoma, mawu anu amatuluka mosajejema komanso mosazengereza kwambiri. Ndiponso, simupunthwapunthwa pa mawu kapena kupwaira malingaliro.

N’chifukwa chiyani kuli kofunikira?

Wokamba nkhani akamadodoma, maganizo a omvera amayamba kuyendayenda; iye angaperekenso malingaliro olakwika. Zimene akunena zingakhale zosakhutiritsa.

KODI mukamaŵerenga mokweza mumapunthwa pa mawu ena? Kapena mukaimirira pamaso pa gulu kuti mulankhule, kodi mumakhala ndi vuto posankha mawu oyenerera? Ngati mumatero, mungakhale ndi vuto la kudodoma. Munthu wosadodoma amaŵerenga ndi kulankhula m’njira yoti mawu ndi malingaliro ake amveke bwinobwino, komanso mosavuta kuwatsatira. Zimenezi sizitanthauza kuti iye amangolankhula mosapumira, kapena kuti amalankhula mothamanga kwambiri, kapena kulankhula mosalingalira ayi. Mawu ake amamveka osangalatsa ndi okoma. Kulankhula mosadodoma kwafotokozedwa bwino kwambiri mu Sukulu ya Utumiki wa Mulungu.

Pali zinthu zosiyanasiyana zimene zingapangitse munthu kumadodoma polankhula. Kodi inuyo mungafunikire kuwongolera pa mbali zotsatirazi? (1) Poŵerengera ena, mungadodome chifukwa cha mawu amene simunawazoloŵere. (2) Kuimaima paliponse kumajejemetsa kaŵerengedwe. (3) Kusakonzekera kungapangitsenso vuto limenelo. (4) Polankhula pamaso pa gulu, chimene chimachititsa kudodoma kaŵirikaŵiri ndi kusayala mfundo m’ndondomeko yabwino. (5) Kusadziŵa kwambiri chinenero kungachititse munthu kudodomadodoma pofunafuna mawu oyenerera. (6) Ngati mutsindika mawu ambiri, mumayamba kulankhula mododoma. (7) Kusadziŵa bwino galamala kungapangitsenso vutolo.

Ngakhale kuti mukulankhula mododoma anthu sangatulukemo mu Nyumba ya Ufumu ayi koma maganizo awo angayambe kuyendayenda. Pachifukwa chimenechi, zambiri zimene munganene zingatayike.

Komanso, m’pofunika kusamala kotero kuti kalankhulidwe kamene kakanakhala kamphamvu ndi kosadodoma kasakhale kolamula, osatinso konyazitsa omvera ayi. Kalankhulidwe kooneka kukhala kamwano kwa anthu ena, kapena komveka kosadalirika chifukwa cha kusiyana kwa zikhalidwe, kamawononga cholinga chanu. Ngakhale kuti mtumwi Paulo anali katswiri wokamba nkhani, onani kuti anafikira Akorinto “mofooka ndi m’mantha, ndi monthunthumira” pokana kudzikweza.—1 Akor. 2:3.

Zizoloŵezi Zoyenera Kupeŵa. Anthu ambiri polankhula amakonda kunena pafupipafupi mawu akuti “ndipo-ee.” Ena amakonda kuyamba chilichonse chimene afuna kunena ndi mawu akuti “choncho,” “mudziŵa,” “mungaone kuti,” ndi ena otero. Mwina simukudziŵa kuti mumatchula mawuŵa kaŵirikaŵiri. Yesani kuti wina azikumvetserani ndipo azibwereza nthaŵi iliyonse pamene muwanena mawuwo. Mukhoza kudabwa.

Anthu ena amakonda kubwerezabwereza poŵerenga. Amayamba sentensi, kenako n’kudzidula okha ndi kuyambiranso zimene anena kale.

Pali ena amene amalankhula bwino, koma vuto lawo n’lakuti amayamba ndi lingaliro ili, kenako chapakati pa sentensi, amasinthira ku lingaliro lina. Ngakhale kuti mawu amatuluka bwinobwino, kusinthasintha malingaliro kumawononga kalankhulidwe kabwino.

Mmene Mungathetsere Vutolo. Ngati vuto lanu ndi kupeza mawu oyenerera, muyenera kuchita khama kuti muphunzire mawu ambiri a chinenerocho. Samalani kwambiri mawu osazoloŵereka mu Nsanja ya Olonda, Galamukani!, ndi mabuku ena amene mumaŵerenga. Yang’anani mawuwo mu mtanthauzira mawu, ndipo awonjezereni pa mawu amene mukuwadziŵa kale. Ngati mulibe mtanthauzira mawu, funsani kwa munthu wina amene amalankhula bwino chinenerocho.

Kukhala ndi chizoloŵezi choŵerenga mokweza nthaŵi zonse kungathandize kuthetsa vutolo. Samalirani mawu ovuta, ndipo muziwatchula mobwerezabwereza.

Kuti muziŵerenga mosadodoma, m’pofunika kudziŵa mmene mawu amagwirira nchito pamodzi m’sentensi. Kaŵirikaŵiri, mawu ayenera kuŵerengedwa m’magulu kuti apereke lingaliro la wolemba. Samalani magulu a mawu oterowo. Ngati kungakuthandizeni, aikeni chizindikiro. Cholinga chanu si kungoŵerenga mawu molondola, koma kuperekanso malingaliro momvekera bwino. Mutapenda sentensi imodzi, pitani pasentensi ina mpaka mutaŵerenga ndime yonse. Dziŵani bwino mgwirizano wa malingalirowo. Kenako yesezani kuŵerenga mokweza. Ŵerengani ndime imodzi mobwerezabwereza kufikira mutakhoza kuŵerenga mosapunthwa ndi mosapumira m’malo olakwika. Ndiyeno pitani pa ndime zina.

Kenako, wonjezerani liŵiro lanu. Ngati mwadziŵa mmene mawu amagwirira ntchito pamodzi m’sentensi, mudzatha kumaona mawu angapo nthaŵi imodzi ndi kudziŵiratu mawu otsatira. Zimenezi zidzathandiza kwambiri kuti muziŵerenga mwaluso.

Kukhala ndi chizoloŵezi choŵerenga mokweza mosakonzekera kungakhale kothandiza. Mwachitsanzo, ŵerengani mokweza lemba la tsiku ndi ndemanga yake popanda kukonzekera; chitani zimenezi nthaŵi zonse. Zoloŵezani maso anu kuona magulu a mawu opereka malingaliro m’malo moona liwu limodzi nthaŵi imodzi.

Kuti mulankhule mosadodoma pokambirana, muyenera kulingalira musanalankhule. Khalani ndi chizoloŵezi chimenecho pamoyo wanu wa tsiku ndi tsiku. Sankhani malingaliro amene mukufuna kunena ndi dongosolo lowanenera; mukatero yambani kulankhula. Musadye mfulumira. Yesetsani kunena ganizo lonse popanda kuima kapena kusintha malingaliro musanamalize ganizolo. N’kothandiza kunena masentensi aafupi ndi osavuta.

Ngati mukudziŵa zimene mukufuna kunena, mawu amatuluka mwachibadwa. Kwenikweni, m’pofunika kusankha mawu amene mukufuna kunena. Pofuna kuzoloŵera, ndi bwino kutsimikiza choyamba m’maganizo mwanu za malingaliro, kenako n’kuganiza za mawu pamene mukulankhula. Ngati mutero, komanso ngati muika maganizo anu pa malingaliro m’malo mwa mawu amene mukulankhula, mawu ake adzabwera mwachibadwa, ndipo mudzawalankhula mochokeradi mumtima. Koma mukangoyamba kuganiza za mawu m’malo mwa malingaliro, kalankhulidwe kanu kadzakhala kododoma. Mwa kuyeseza, mukhoza kupambana pakulankhula mosadodoma, kumene ndiko mbali yofunika kwambiri ya kulankhula ndi kuŵerenga mogwira mtima.

Pamene Mose anatumidwa kukaimira Yehova ku mtundu wa Israyeli ndi pamaso pa Farao wa ku Igupto, anaona kuti sakanatha. Chifukwa chiyani? Sanali kutha kulankhula bwinobwino; mwina anali ndi vuto lachibadwa. (Eks. 4:10; 6:12) Mose anapereka zifukwa zodzikhululukira, koma Mulungu sanavomereze n’chimodzi chomwe. Yehova anatumiza Aroni kukhala wolankhulira Mose, koma anathandizanso Mose kulankhula. Mobwerezabwereza komanso mogwira mtima, Mose analankhula osati chabe kwa mmodzi ndi mmodzi wa anthu, komanso ku timagulu ta anthu, ndi ku mtundu wonse. (Deut. 1:1-3; 5:1; 29:2; 31:1, 2, 30; 33:1) Inunso ngati mulimbikira mbali yanu ndi mtima wonse podalira Yehova, mukhoza kugwiritsa ntchito luso lanu la kulankhula kulemekezera Mulungu.

KUTHANA NDI CHIBWIBWI

Ndi zinthu zambiri zimene zimachititsa chibwibwi. Njira zimene zimathandiza anthu ena achibwibwi sizigwira ntchito kwa ena. Koma kuti mupeze chimwemwe pothana ndi chibwibwi, m’pofunika kulimbikira.

Kodi mumagwidwa ndi mantha kapena nkhaŵa pofuna kupereka ndemanga pamsonkhano? Pempherani kwa Yehova kuti akuthandizeni. (Afil. 4:6, 7) Ikani maganizo anu pa kulemekeza Yehova ndi kuthandiza ena. Musayembekeze kuti vutolo lidzatheratu, koma tsatirani malangizo a mmene mungathanire nalo. Mmene mukulandira dalitso la Yehova ndi chilimbikitso chochokera kwa abale, limbikiranibe.

Sukulu ya Utumiki wa Mulungu imapereka mwayi wophunzira kulankhula pamaso pa gulu. Mungadabwe kuona mmene mungachitire bwino pamaso pa gulu lokulimbikitsani ndi lofuna kuti mupambane. Zimenezi zingakuthandizeni kukhala ndi chidaliro cholankhula m’mikhalidwe inanso.

Ngati mwapatsidwa nkhani yokakamba, konzekerani bwinobwino. Ikani mtima wonse m’nkhani yanu. Lankhulani ndi mzimu waubwenzi. Ngati muyamba kuchita chibwibwi m’kati mwa nkhani, yesetsani kulankhula modekha ndi kukhazika mtima pansi. Masulani nyama za m’nsagwada. Nenani masentensi afupiafupi. Yesani kuchepetsa mawu akuti “mm” ndi “ee.”

Podziŵa mawu amene amawavuta kutchula, anthu amene ali ndi chibwibwi amayesa kupeŵa mawuwo, m’malo mwake, amatchula mawu ena ofanana tanthauzo. Ena amakonda kudziŵa mawu amene amawavuta kwambiri pofuna kuti aziwayeseza mobwerezabwereza.

Ngati mumachita chibwibwi polankhula, musasiye kuyesetsa kwanu kukambirana ndi anthu. Limbikitsani winayo kuti apitirize kulankhula kufikira mutakonzeka kulankhulanso. Ngati kuli kofunika, tangolembani papepala kapena onetsani munthuyo mawu olembedwa.

MMENE MUNGACHITIRE ZIMENEZO

  • Poŵerenga magazini ndi mabuku, lembani mzera kunsi kwa mawu atsopano, pezani matanthauzo ake, kenako agwiritseni ntchito.

  • Yesezani kuŵerenga mokweza kwa mphindi faifi mpaka teni tsiku lililonse.

  • Konzekerani bwino lomwe mbali zoŵerenga. Zindikirani mwapadera magulu a mawu opereka ganizo. Dziŵani bwino mgwirizano wa malingaliro.

  • Pokambirana ndi anthu tsiku ndi tsiku, phunzirani kuganiziratu choyamba, kenako nenani sentensi yonse osaima.

ZOCHITA: Ŵerengani mumtima ndi mosamala Oweruza 7:1-25, mukumayesetsa kupenda ndime imodzi imodzi. Tsimikizani kuti mukumvetsa zimene ikunena. Mwa kugwiritsa ntchito mtanthauzira mawu, pezani tanthauzo la mawu amene simuwadziŵa. Kenako ŵerengani ndimeyo mokweza; komanso molondola kwambiri. Mukakhutira ndi ndimeyo, pitani ku yotsatira, choncho basi. Ndiyeno ŵerengani chaputala chonse. Bwerezani zimenezo, koma tsopano mofulumirirapo. Bwerezaninso, koma mofulumirirapo kwambiri m’malo oyenerera—koma osathamanga kwambiri moti muchite kupunthwa.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena