Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • be phunziro 16 tsamba 135-tsamba 138 ndime 4
  • Kudekha

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Kudekha
  • Pindulani ndi Sukulu ya Utumiki wa Mulungu
  • Nkhani Yofanana
  • Kukhazikika Maganizo ndi Maonekedwe a Munthu
    Buku Lolangiza la Sukulu ya Utumiki Wateokalase
  • Kodi Ndingathe Bwanji Kukamba Nkhani Bwino Pagulu?
    Galamukani!—2004
  • Mfundo Zopatsa Chidziŵitso, Zofotokozedwa Momveka Bwino
    Buku Lolangiza la Sukulu ya Utumiki Wateokalase
  • Mawu Oyamba Okopa Chidwi
    Pindulani ndi Sukulu ya Utumiki wa Mulungu
Onani Zambiri
Pindulani ndi Sukulu ya Utumiki wa Mulungu
be phunziro 16 tsamba 135-tsamba 138 ndime 4

PHUNZIRO 16

Kudekha

Kodi muyenera kuchita motani?

Muyenera kuima, kusuntha, ndi kulankhula mofatsa ndi mwaulemu moonetsa kukhazikika maganizo.

N’chifukwa chiyani kuli kofunikira?

Ngati muli odekha, omvera anu adzaika maganizo pa zimene mukunena osati pa inu.

SI CHACHILENDO ngati wokamba nkhani amva mantha ena ake pamene anyamuka kuti akakambe nkhani, makamaka ngati sakamba nkhani kaŵirikaŵiri. Wofalitsa angamve mantha ena ake pamene alalikira makomo angapo kwa nthaŵi yoyamba mu utumiki wa kumunda. Pamene Yeremiya anaikidwa mneneri, anati: “Sindithayi kunena pakuti ndili mwana.” (Yer. 1:5, 6) Yehova anathandiza Yeremiya, inunso akuthandizani. M’kupita kwa nthaŵi, muzilankhula modekha.

Wokamba nkhani modekha amakhala wokhazikika maganizo. Kufatsa kumeneku kumaoneka ndi mmene amaimira. Kaimidwe kake kamakhala kachibadwa ndi koyenerera chochitikacho. Amagwiritsa ntchito manja ake mwatanthauzo. Mawu ake amakhala otsindika ndi ofatsa.

Ngakhale kuti mungaone kuti mukupereŵera pa malongosoledwe a munthu wodekha ameneŵa, mukhoza kuwongolera. Motani? Tiyeni tione chimene chimachititsa wokamba nkhani kuchita mantha ndi kusadekha. Chochititsa chingakhale mmene thupi limagwirira ntchito.

Ngati mwakumana ndi vuto linalake ndipo mukufuna kuti muthane nalo koma mukukayika, nkhaŵa imakugwirani. Zimenezo zikachitika, ubongo umachititsa kachiwalo kena ka m’thupi kutulutsa madzi ena ake otchedwa adrenaline. Madziwo akamatuluka ambiri angachititse mtima kugunda mofulumira kwambiri, kusintha kapumidwe, kuwonjezera thukuta, ngakhalenso kunjenjemeretsa manja ndi mawondo, mawunso angatuluke onjenjemera. Thupi lanu limayesetsa kukuthandizani kuthana ndi vutolo mwa kuwonjezera nyonga yanu. Vuto limakhala pa kugwiritsa ntchito nyongayo kuti ikuthandizeni kulingalira bwino ndi kulankhula modekha.

Mmene Mungachepetsere Nkhaŵa. Kumbukirani kuti kukhala ndi nkhaŵa inayake n’chibadwa. Komabe, kuti mukhale wodekha muyenera kuchepetsa nkhaŵayo ndi kuthana ndi vutolo m’njira yofatsa ndi yodzilemekeza. Kodi mungachite motani zimenezo?

Konzekerani bwino. Patulani nthaŵi yokonzekera nkhani yanu. Onetsetsani kuti nkhaniyo mukuimvetsa bwino. Ngati nkhani yanu ndi yofotokoza mfundo zimene mwasankha, ganizirani zimene omvera anu akudziŵa kale pankhaniyo ndi zimene mukufuna kukwaniritsa. Izi zidzakuthandizani kusankha mfundo zopindulitsa kwambiri. Ngati poyamba zikukhala zovuta, kambiranani vutolo ndi wokamba nkhani wozoloŵera. Angakuthandizeni kulingalira bwino za mfundo zanu ndi omvera anu. Ngati mwatsimikiza kuti mwapeza mfundo zothandiza omvera anu ndipo mwazimvetsa bwino, kufunitsitsa kwanu kuzifotokoza kudzaphimba nkhaŵa imene munali nayo.

Ganizirani mofatsa za mawu anu oyamba. Dziŵani mmene mungayambire. Nkhani yanu ili m’kati, mantha anu adzatha.

Masitepe amenewo amagwiranso ntchito pokonzekera utumiki wa kumunda. Musalingalire ulaliki wokha umene mukaupereke, komanso mtundu wa anthu amene mukawalalikirewo. Konzani mawu oyamba mosamala. Onerani kwa ofalitsa ofikapo odziŵa zambiri.

Mwina mungaganize kuti kuti mukalankhule modekha pamaso pa gulu, nkhani yanu muyenera kuilemba yonse kuti ikhale yoŵerenga. Zimenezi zingangowonjezera nkhaŵa yanu nthaŵi iliyonse pamene mukamba nkhani. N’zoona kuti okamba nkhani ena amalemba manotsi ochuluka kwambiri, pamene ena amalemba ochepa. Koma chimene chingakuthandizeni pankhani yanu kuti muchepetse nkhaŵa, si mawu a papepala ayi, koma chidaliro cha mumtima mwanu chakuti zimene mwakonzera omvera anu n’zopindulitsadi.

Yesezani nkhani yanu mwa kulankhula momveka. Kuyeseza koteroko kudzakupatsani chidaliro chakuti mukhoza kulankhula zimene mukulingalira. Pamene mukuyeseza, mumaloŵetsa zinthu m’maganizo zimene zimakumbukika pokamba nkhani. Pokonzekera yesezani zenizeni. Muziwaona omvera anu m’maganizo. Khalani pathebulo kapena imani pasitandi, mmene mukachitire pokamba nkhani yanu.

Pempherani kwa Yehova kuti akuthandizeni. Kodi iye angayankhe pemphero ngati limenelo? “Uku ndi kulimbika mtima kumene tili nako kwa Iye, kuti ngati tipempha kanthu monga mwa chifuniro chake, atimvera.” (1 Yoh. 5:14) Ngati mukufuna kulemekeza Mulungu ndi kuthandiza anthu kuti apindule ndi Mawu ake, ndithudi adzayankha pemphero lanu. Chidaliro chimenecho chingakulimbikitseni kwambiri kuti mukakambe nkhani yanu modekha. Ndiponso, pamene mukulitsa zipatso za mzimu—chikondi, chimwemwe, mtendere, chifatso, ndi kudziletsa—mudzakhala ndi maganizo ofunikira posamalira zinthu modekha.—Agal. 5:22, 23.

Zoloŵerani. Mukamaloŵa mu utumiki wa kumunda kaŵirikaŵiri, mantha anu adzachepa. Ndipo mukamayankha kaŵirikaŵiri pamisonkhano ya mpingo, kudzakhala kosavuta kulankhula kwa anthu ena. Mukamakamba nkhani mumpingo mobwerezabwereza, nkhaŵa imene mumakhala nayo musanakambe nkhani iliyonse idzacheperachepera. Kodi mungakonde kukhala ndi mipata yambiri yokamba nkhani? Pamenepo muzikonzekera kukamba nkhani zogwirizira m’sukulu pamene eniake alephera kukwaniritsa mbali zawo.

Mutatsatira masitepe omwe talongosolaŵa, mudzaona kuti ndi bwino kuona zizindikiro zosonyeza kusakhazikika maganizo. Kudziŵa zizindikirozo ndi mmene mungathanire nazo kudzakuthandizani kulankhula modekha. Zizindikirozo zingakhale za thupi kapena za m’mawu.

Zizindikiro za Thupi. Kudekha kwanu, kapena kusadekha, kumaoneka mwa kaimidwe ka thupi lanu ndi mmene mukugwiritsira ntchito manja anu. Choyamba lingalirani manja. Kufumbata manja kumbuyo, kuika manja m’mbali momangika ngati papelete, kapena kugwira mwamphamvu sitandi yolankhulirapo; kupisa ndi kutulutsa manja m’matumba mobwerezabwereza, kumanga ndi kumasula mabatani a jekete, kugwiragwira chibwano popanda chifukwa, kugwiragwira mphuno, magalasi amaso; kuseŵeretsa wotchi, pensulo, mphete, kapena autilaini; kulankhula ndi manja konjenjemera kapena kosamalizitsa polankhula—zonsezi zimaonetsa kusadekha.

Kusadekha kungaonekerenso mwa kusunthasuntha miyendo, kuyendetsa thupi uku ndi uku, kuima momangika kwambiri, kuima mosawongoka bwino, kunyambita milomo kaŵirikaŵiri, kumezameza mate kapena kuti malovu, ndi kupuma mofulumira ndi mosakoka mpweya wambiri.

Mwa kuyesetsa mwakhama, mukhoza kulamulira zizindikiro za mantha zonsezi. Limbikirani kuthana ndi chimodzi panthaŵi imodzi. Dziŵani chimene chili vuto, ndipo lingalirani pasadakhale zimene muyenera kuchita kuti musachite zimenezo. Ngati muchita khama limenelo, mudzaonetsa kudekha m’kaimidwe ka thupi lanu.

Zizindikiro za M’mawu. Zizindikiro za m’mawu za kusadekha zingaphatikizepo kukweza mawu kwambiri kapena mawu onjenjemera. Mwina mumakhosomola kapena kuti kutsokomola kaŵirikaŵiri poyeretsa pakhosi kapena mumalankhula mofulumira kwambiri. Mavuto ndi zizoloŵezi zimenezi mungazigonjetse mwa kulamulira mawu anu mwakhama.

Ngati mukuchita mantha, pumani mpweya wambiri kangapo musanapite kupulatifomu. Yesani kumasula thupi lanu lonse. M’malo moganizira za mantha anu, lingalirani za chifukwa chimene mukufunira kufotokozera omvera anu zimene mwawakonzera. Mukafika papulatifomu, imani kaye pang’ono ndi kuyang’ana omvera anu musanayambe kulankhula. Kenako, pezani nkhope yaubwenzi ndipo mwetulirani. Lankhulani mawu oyamba pang’onopang’ono, kenako loŵererani m’nkhani yanu.

Zimene Muyenera Kuyembekezera. Musayembekezere kuti mantha anu adzatheratu onse. Ambiri omwe akhala akukamba nkhani zaka zambiri papulatifomu amamvabe mantha ena ake asananyamuke kukaimirira pamaso pa gulu. Komabe, iwo aphunzira kulamulira mantha awo. Wina mwa oterowo anati: “Ndimakhalabe ndi mantha, koma tsopano ndimatha kuwalamulira.”

Ngati muyesetsa ndi mtima wonse kuthetsa zizindikiro za mantha, omvera anu azikuonani monga wokamba nkhani wodekha. Mungamavebe timantha ndithu, koma iwo sangazindikire zimenezo m’pang’ono pomwe.

Kumbukirani, kuwonjezeka kwa madzi am’thupi aja otchedwa adrenaline omwe amachititsa zizindikiro za mantha kumawonjezeranso nyonga. Gwiritsani ntchito nyongayo polankhula mwaumoyo.

Musachite kuyembekeza nthaŵi yodzapita kupulatifomu kuti mukayeseze zinthu zimenezi. Phunzirani kukhala wodekha ndi wokhazikika maganizo ndi kulankhula ndi mzimu woyenerera monga mwa malankhulidwe anu a tsiku ndi tsiku. Kuchita zimenezo kudzakuthandizani kwambiri kukhala ndi chidaliro papulatifomu ndi mu utumiki wa kumunda, kumene lusolo lili lofunika kwambiri.

MMENE MUNGAPEZERE LUSO LA KUDEKHA

  • Konzekerani bwino.

  • Yesezani nkhani zanu mwa kulankhula momveka.

  • ‘Msenzeni Yehova nkhaŵa zanu’ m’pemphero.—Sal. 55:22.

  • Loŵani mu utumiki wa kumunda nthaŵi zonse, yankhani kaŵirikaŵiri pa misonkhano, ndipo muzikonzekera kukamba nkhani zogwirizira m’sukulu.

  • Dziŵani zizindikiro za kusakhazikika maganizo, ndipo dziŵaninso kuzipeŵa kwake kapena kuzilamulira kwake.

ZOCHITA: Mlungu uliwonse kwa mwezi umodzi, yesetsani kuyankha koposa kamodzi pa Phunziro la Nsanja ya Olonda ndi pa Phunziro la Buku la Mpingo. Dziŵani kuti mantha amayamba kuchepa mukayankha kachiŵiri kapena kachitatu pamsonkhano uliwonse.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena