PHUNZIRO 23
Kumveketsa Phindu la Nkhani Yanu
KAYA mukulankhula kwa munthu mmodzi kapena kwa anthu ambiri, musaganize kuti anthuwo akhala ndi chidwi pankhani yanu kokha chifukwa inuyo muli nayo chidwi. Inde uthenga wanu ndi wofunika, koma ngati simumveketsa bwino phindu lake, chidwi cha omvera chingazilale.
Zimakhaladi choncho ngakhale kwa omvera mu Nyumba ya Ufumu. Iwo angatchere khutu pamene mugwiritsa ntchito fanizo kapena chochitika chimene sanamvepo. Koma angasiye kumvetsera mukayamba kulankhula nkhani imene akuidziŵa kale, makamaka mukalephera kufotokoza m’njira yatsopano mfundo zimene akuzidziŵa kale pankhaniyo. Athandizeni kuona chifukwa chake zimene mukunenazo zili zothandiza ndi kuwafotokozera phindu lake.
Baibulo limatilimbikitsa kulingalira zinthu zopindulitsa. (Miy. 3:21) Yehova anagwiritsa ntchito Yohane Mbatizi kuonetsa anthu “nzeru ya olungama mtima.” (Luka 1:17) Imeneyi ndi nzeru yochokera m’mantha akulemekeza Yehova. (Sal. 111:10) Awo amene amazindikira nzeru imeneyi amakhoza kuthana ndi zovuta za moyo uno ndi kugwira zolimba moyo weniweni, moyo wosatha ukudzawo.—1 Tim. 4:8; 6:19.
Kupangitsa Nkhani Kukhala ya Phindu. Kuti nkhani yanu ikhale yopindulitsa, lingalirani mosamala mfundo zanu, komanso omvera anu. Musawaone ngati gulu chabe la anthu. Onani kuti mwa omverawo muli anthu osiyanasiyana komanso mabanja. Mungakhalenso ana achichepere, achinyamata, achikulire, ndi ena okalamba. Mungakhalenso okondwerera atsopano komanso aja amene anayamba kutumikira Yehova inuyo musanabadwe. Ena angakhale okhwima mwauzimu; ena angakhalebe ndi maganizo ndi machitachita ena a dzikoli. Dzifunseni kuti: ‘Kodi nkhani imene ndikakambeyi ikawapindulitsa motani omvera? Kodi ndingakawathandize motani kumvetsa mfundo yake yaikulu?’ Mwina mungaganize zolunjikitsa kwambiri nkhani yanu ku gulu limodzi kapena aŵiri mwa anthu omwe tatchulawo. Komabe, musaiwaliretu enawo.
Bwanji ngati mwapatsidwa nkhani yoti mufotokoze chimodzi cha ziphunzitso zazikulu za m’Baibulo? Kodi nkhani imeneyo mungaikambe motani kuti ipindulitse omvera amene amakhulupirira kale chiphunzitsocho? Yesetsani kulimbikitsa chikhulupiriro chawo. Motani? Mwa kufotokoza umboni wa m’Malemba wovomereza chiphunzitsocho. Mukhoza kuwathandizanso kuzamitsa chidziŵitso chawo pa chiphunzitso cha Baibulo chimenecho. Mungachite zimenezi mwa kusonyeza mmene chiphunzitsocho chimagwirizanira ndi mfundo zina za choonadi cha Baibulo komanso ndi mkhalidwe wa Yehova. Gwiritsani ntchito zitsanzo—zochitika zenizeni ngati n’kotheka—zosonyeza kuti kumvetsa chiphunzitso chimenechi kwathandizadi anthu, ndi mmene chimathandizira munthu kuyang’ana m’tsogolo ndi chidaliro.
Kuonetsa mmene mfundo zimagwirira ntchito musakufotokoze m’mawu omaliza okha a nkhani yanu. Kuchokera pachiyambi pa nkhani yanu, womvera aliyense ayenera kunena mumtima mwake kuti “izi zikundikhudza.” Pokhala mutayala maziko amenewo, pitirizani kusonyeza mmene mfundo yaikulu iliyonse m’nkhaniyo ikugwirira ntchito. Teroninso m’mawu omaliza.
Posonyeza mmene mfundo zikugwirira ntchito, samalani kuti muchite mogwirizana ndi mfundo za makhalidwe abwino za m’Baibulo. Kutanthauza chiyani? Kutanthauza kuchita zimenezo m’njira yachikondi ndi yosonyeza chifundo. (1 Pet. 3:8; 1 Yoh. 4:8) Ngakhale pamene mtumwi Paulo anali kusamalira mavuto aakulu ku Tesalonika, anagogomeza kwambiri mbali zolimbikitsa abale ndi alongo ake achikristu kupita patsogolo mwauzimu. Anasonyezanso kuti anali ndi chidaliro chakuti iwo akakhala ofunitsitsa kuchita zoyenera m’nkhani imene anakambirana nawo. (1 Ates. 4:1-12) Chitsanzo chabwino kwambiri choti ifenso titengere!
Kodi cholinga cha nkhani yanu ndi kulimbikitsa ntchito yolalikira ndi kuphunzitsa ena uthenga wabwino? Pamenepo alimbikitseni kuti azikhala osangalala ndi oyamikira mwayi umenewo. Komabe, musaiwale kuti anthu angathe kugwira ntchito imeneyo pamlingo wosiyanasiyana; Baibulonso limavomereza zimenezo. (Mat. 13:23) Musachititse abale anu kukhala ndi maganizo odziimba mlandu. Pa Ahebri 10:24 timalimbikitsidwa kuti “tifulumizane ku chikondano ndi ntchito zabwino.” Ngati tifulumiza ena ku chikondano, adzatha kugwira ntchito ndi cholinga chabwino. Kusiyana ndi kuumirira kuti onse azichita zinthu mofanana, zindikirani kuti chimene Yehova amafuna n’chakuti ife tilimbikitse ‘kumvera mwa chikhulupiriro.’ (Aroma 16:26) Pokumbukira zimenezi, tidzayesetsa kulimbikitsa chikhulupiriro chathu ndi cha abale athu.
Kuthandiza Ena Kuona Phindu la Nkhani Yanu. Pamene mulalikira kwa ena, musalephere kumveketsa phindu lenileni la uthenga wabwino. Kuti mukathe kuchita zimenezo muyenera kulingalira zimene zili m’maganizo mwa anthu a m’gawo lanu. Kodi mungadziŵe bwanji? Mverani nkhani pawailesi ya mawu kapena ya kanema. Yang’anani nkhani zosonyezedwa patsamba loyamba la nyuzipepala. Ndiponso, yesetsani kukambirana ndi anthu, ndipo mvetserani pamene akulankhula. Mungapeze kuti iwo akulimbana ndi mavuto akutiakuti, monga kuchotsedwa ntchito, kusoŵa ndalama zalendi, matenda, imfa ya wina m’banja, kuopa zigawenga, kuchitidwa mopanda chilungamo ndi wina waudindo, kutha kwa ukwati, kupulupudza kwa ana, ndi zina zotero. Kodi Baibulo lingawathandize? Ndithudi lingawathandize.
Poyamba kukambirana, mwachidziŵikire mudzakhala ndi nkhani inayake m’maganizo mwanu. Komabe, ngati munthuyo aonetsa kuti ali ndi nkhani ina yofuna kukambirana msanga, kambiranani imeneyo ngati mungathe kutero. Apo ayi pemphani kuti mukabwere ndi mfundo zothandiza. N’zoona kuti timakana ‘kuloŵerera nkhani zosatikhudza,’ komabe timakonda kugaŵana ndi ena uphungu wothandiza wochokera m’Baibulo. (2 Ates. 3:11, NW) Inde, uphungu umene anthu angakonde kwambiri kuumva ndi uphungu wa m’Baibulo umene umakhudza miyoyo yawo.
Anthu akapanda kuona mmene uthenga wathu ukuwakhudzira, nthaŵi zina amangothetsa kukambiranako. Ngakhale atatilola kulankhula, ngati tilephera kusonyeza phindu lenileni la nkhani yathu, uthenga wathuwo sungakhudze miyoyo yawo kwenikweni. Koma ngati timveketsa bwino lomwe phindu la uthengawo, kukambiranako kungakhale chiyambi cha kusintha kwa moyo wa munthuyo.
Pochititsa maphunziro a Baibulo, pitirizani kuunika phindu lenileni la phunzirolo. (Miy. 4:7) Athandizeni ophunzira kuti amvetse uphungu wa m’Malemba, mfundo za makhalidwe abwino, ndi zitsanzo zowasonyeza mmene angayendere m’njira za Yehova. Tsindikani mapindu amene amakhalapo pochita motero. (Yes. 48:17, 18) Zimenezo zidzalimbikitsa ophunzirawo kusintha mbali zofunikira kusintha m’miyoyo yawo. Mangani mwa iwo chikondi cha pa Yehova ndi chikhumbo chofuna kum’kondweretsa. Ndipo athandizeni kukhala ndi mtima wofunitsitsa kugwiritsa ntchito uphungu wochokera m’Mawu a Mulungu.