Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • be phunziro 28 tsamba 179-tsamba 180 ndime 7
  • Kukamba Nkhani Mmene Mumalankhulira ndi Anthu

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Kukamba Nkhani Mmene Mumalankhulira ndi Anthu
  • Pindulani ndi Sukulu ya Utumiki wa Mulungu
  • Nkhani Yofanana
  • Kulankhula Nkhani Mosadodoma, Mokambirana Komanso Motchula Bwino Mawu
    Buku Lolangiza la Sukulu ya Utumiki Wateokalase
  • Kulankhula Mwachibadwa
    Pindulani ndi Sukulu ya Utumiki wa Mulungu
  • Kukhala ndi Kalankhulidwe Kabwino Tsiku ndi Tsiku
    Buku Lolangiza la Sukulu ya Utumiki Wateokalase
  • Kulankhula Mokambirana ndi Anthu
    Kuwerenga Komanso Kuphunzitsa Mwaluso
Onani Zambiri
Pindulani ndi Sukulu ya Utumiki wa Mulungu
be phunziro 28 tsamba 179-tsamba 180 ndime 7

PHUNZIRO 28

Kukamba Nkhani Mmene Mumalankhulira ndi Anthu

Kodi muyenera kuchita motani?

Lankhulani mmene mumalankhulira ndi anthu masiku onse koma moyenerera omvera anu.

N’chifukwa chiyani kuli kofunikira?

Kukamba nkhani mmene mumalankhulira ndi anthu masiku onse kumamasula omvera anu ndipo kumawapatsa chidwi chomvetsera zimene mukunena.

KAŴIRIKAŴIRI anthu amakhala omasuka pokambirana ndi anzawo. Mawu awo amatuluka mwachibadwa. Anthu ena amalankhula kwambiri; ena ndi ofatsirapo. Mulimonsemo, kulankhula mwachibadwa kumakopa chidwi.

Komabe, pofikira munthu amene simum’dziŵa, n’kosayenera kulankhula naye momasuka kwambiri ngati kuti munazoloŵerana naye. Ndipo kumadera ambiri, kukambirana kulikonse ndi munthu wosam’dziŵa kumayamba mwaulemu kwambiri. Mutapereka ulemu woyenererawo, mumayamba kulankhula momasukirapo kenako mumakambirana momasuka.

Polankhula pa pulatifomu, muyeneranso kusamala. Kulankhula momasuka kwambiri kumachepetsa ulemu wa msonkhano wachikristu komanso ukumu wa zimene mukunena. M’zinenero zina, alipo mawu oyenera kutchula polankhula ndi munthu wachikulire, mphunzitsi, mkulu wa boma, kapena kholo. (Onani mawu ogwiritsidwa ntchito pa Machitidwe 7:2 ndi 13:16.) Palinso mawu ena owatchula polankhula ndi mkazi wanu kapena mwamuna wanu kapenanso mnzanu wokondana naye. Ngakhale kuti kalankhulidwe ka papulatifomu sikayenera kukhala komangika kwambiri, kazikhalabe kaulemu.

Komanso, zilipo zinthu zina zimene zingachititse kakambidwe ka munthu kukhala komangika kwambiri. Chimodzi mwa zinthuzo ndi kapangidwe ka masentensi, kapena kuti ziganizo. Pamakhala vuto ngati wokambayo akuyesa kulankhula masentensiwo ndendende mmene alembedwera. Mawu olembedwa kaŵirikaŵiri amatuluka mosiyana ndi ongolankhula. N’zoona kuti pokonzekera nkhani timaifufuza mwa kuŵerenga mawu olembedwa kale. Komanso timakhala ndi autilaini yolembedwa monga maziko a nkhani yathu. Koma ngati m’nkhani yanu mulankhula maganizo ndendende mmene alembedwera, kapena ngati mungoŵerenga pa autilaini yosindikizidwa, kakambidwe kanu sikangamveke mmene mumalankhulira masiku onse. Kuti kakambidwe kanu kamveke mmene mumalankhulira ndi anthu, lankhulani maganizo anu m’mawu anuanu ndipo peŵani masentensi ovuta.

Chofunika china ndi kusinthasintha liŵiro la kalankhulidwe. Wokamba nkhani akamalankhula momangika, kaŵirikaŵiri amatchula mawu molinganizika kwambiri ndipo liŵiro limakhala lofanana m’nkhani yonseyo. M’kukambirana kwa masiku onse, timasinthasintha liŵiro ndipo timapumira mosiyanitsasiyanitsa.

Komabe, pamene mulankhula pamaso pa gulu lalikulu, powonjezera pa kulankhula monga mwa masiku onse, muyeneranso kukweza mawu, kuwonjezera mphamvu ya mawu, kulankhula mwaumoyo kuti mukope chidwi cha omverawo.

Kuti mu utumiki wa kumunda mukalankhule mmene mumalankhulira mwachibadwa, muyenera kuyesetsa kumalankhula bwino masiku onse. Apa sitikutanthauza kuti muyenera kukhala wophunzira kwambiri ayi. Koma ndi chinthu chabwino kukhala ndi chizoloŵezi cholankhula bwino chimene chingapangitse ena kumvetsera mwaulemu zimene munena. Ndi mfundo zimenezo, onani ngati mufunikira kukonza mbali zina pa mfundo zotsatirazi m’kalankhulidwe kanu ka tsiku ndi tsiku.

  1. Pewani mawu osokoneza kalankhulidwe kabwino kapena kotengera anthu amene moyo wawo umanyoza makhalidwe oopa Mulungu. Mogwirizana ndi uphungu wa pa Akolose 3:8, pewani mawu onyoza ndi otukwana. Mawu amene anthu amalankhula mwa masiku onse ali bwino kuwagwiritsa ntchito. Mawu oterowo ndi omasuka kwambiri, koma akhale mawu abwino ndi ololeka.

  2. Pewani kubwerezabwereza mawu amodzimodzi pofotokoza mfundo zosiyanasiyana. Phunzirani kugwiritsa ntchito mawu omveketsa bwino zimene mukutanthauza.

  3. Pewani kuphimba mfundo zabwino ndi mawu ambirimbiri. Khalani ndi chizoloŵezi cholankhula m’mawu osavuta mfundo imene mukufuna kuti akaikumbukire.

  4. Lankhulani m’njira yosonyeza ena ulemu.

MMENE MUNGALIPEZERE LUSO LIMENELI

  • Yambani mwa kuganizira omvera anu. Aoneni ngati mabwenzi anu, koma musawamasukire kwambiri. Chitani nawo mwaulemu.

  • Lankhulani mochokera mu mtima. Musalankhule mawu onse mmene alembedwera. Lankhulani maganizowo m’mawu anu. Nenani masentensi afupiafupi, ndipo alankhuleni pa liŵiro losiyanasiyana.

  • Maganizo anu akhale pa kugaŵira uthengawo. Lankhulani zochokera pansi pa mtima. Chofunika kwambiri ndicho uthengawo, osati kuti mutchuke ayi.

  • Konzani kalankhulidwe kanu ka masiku onse. Limbikirani pa mfundo zimene zaperekedwa pa tsamba lino, imodzi ndi imodzi.

ZOCHITA: Onani kuti pokambirana mumachita motani. Limbikirani pa mfundo zisanu zimene tandandalika pamwambapa, ndipo tengani imodzi pa tsiku limodzi. Nthaŵi iliyonse pamene mulakwitsa, bwerezaninso ganizo lanu m’mawu anu, koma panthaŵiyo molondola.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena