Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • jy mutu 16 tsamba 42-tsamba 43 ndime 8
  • Yesu Anali Wodzipereka pa Kulambira Mulungu

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Yesu Anali Wodzipereka pa Kulambira Mulungu
  • Yesu—Ndi Njira, Choonadi ndi Moyo
  • Nkhani Yofanana
  • Changu cha Kulambira Yehova
    Munthu Wamkulu Woposa Onse Amene Anakhalako
  • Yesu Anayeretsa Kachisi
    Zimene Tingaphunzire Munkhani za M’Baibulo
  • Chozizwitsa Chachiwiri Chimene Yesu Anachita ku Kana
    Yesu—Ndi Njira, Choonadi ndi Moyo
  • Chozizwitsa Choyamba Chimene Yesu Anachita
    Yesu—Ndi Njira, Choonadi ndi Moyo
Onani Zambiri
Yesu—Ndi Njira, Choonadi ndi Moyo
jy mutu 16 tsamba 42-tsamba 43 ndime 8
Yesu akuthamangitsa osintha ndalama m’kachisi

MUTU 16

Yesu Anali Wodzipereka pa Kulambira Mulungu

YOHANE 2:12-22

  • YESU ANAYERETSA KACHISI

Atachoka ku ukwati wa ku Kana, Yesu analowera ku Kaperenao. Pa ulendowu Yesu anali ndi mayi ake komanso abale ake omwe mayina awo anali Yakobo, Yosefe, Simoni ndi Yuda.

Koma n’chifukwa chiyani Yesu anapita ku Kaperenao? Mzinda wa Kaperenao unali waukulu komanso wodziwika kuposa mzinda wa Nazareti kapena wa Kana. Komanso ophunzira ambiri a Yesu ankakhala mumzinda umenewu kapena chakufupi ndi mzindawu ndipo Yesu akanatha kuwaphunzitsa zinthu zina ali kwawo.

Pa nthawi imene Yesu anali ku Kaperenao anachita zinthu zozizwitsa. Choncho anthu ambiri a mumzindawu ndi madera ena ozungulira anamva zimene Yesu anachita kumeneko. Koma Yesu ndi ophunzira ake, omwe anali Ayuda odzipereka, sanakhalitse mumzindawo. Iwo ananyamuka kupita ku Yerusalemu kuti akachite nawo mwambo wa Pasika wa mu 30 C.E.

Atafika kukachisi ku Yerusalemu, ophunzirawo anaona Yesu akuchita zinthu zodabwitsa kwambiri zimene anali asanachitepo.

Pa nthawiyi Chilamulo cha Mulungu chinkanena kuti Aisiraeli azipereka nsembe za nyama pakachisi. Koma panali anthu ena omwe ankachokera kutali omwe ankafunika kugula zakudya komanso zinthu zina zofunikira pa nthawi yonse imene ankakhala ku Yerusalemuko. Choncho Chilamulo chinkalola anthu amenewa kubweretsa ndalama zimene ankagulira “ng’ombe, nkhosa, mbuzi,” komanso zinthu zina. (Deuteronomo 14:24-26) Chifukwa cha zimenezi, amalonda a ku Yerusalemu ankagulitsa nyama kapena mbalame mkati mwa bwalo la kachisiyo, zimene anthu ankapereka nsembe. Ena mwa amalondawa ankabera anthu powagulitsa zinthuzi pa mtengo wokwera kwambiri.

Yesu ataona zimenezi anakwiya kwambiri ndipo anakhuthula makobidi a osintha ndalama, kugubuduza matebulo awo n’kuwathamangitsa. Kenako Yesu anauza anthuwo kuti: “Chotsani izi muno! Mulekeretu kusandutsa nyumba ya Atate wanga kukhala nyumba ya malonda.”—Yohane 2:16.

Ophunzira a Yesu ataona zimenezi anakumbukira ulosi wonena za Mwana wa Mulungu womwe unanena kuti: “Kudzipereka kwambiri panyumba yanu kudzandidya.” Koma Ayuda anafunsa kuti: “Utionetsa chizindikiro chotani tsopano chosonyeza kuti uli ndi ulamuliro wochitira zinthu zimenezi?” Yesu anayankha kuti: “Gwetsani kachisi uyu, ndipo ine ndidzamumanga m’masiku atatu.”—Yohane 2:17-19; Salimo 69:9.

Ayuda ankaganiza kuti Yesu ankanena za kachisi weniweni amene anali ku Yerusalemu, choncho anafunsa kuti: “Kachisi ameneyu anamumanga zaka 46, ndiye iwe udzamumanga m’masiku atatu?” (Yohane 2:20) Koma Yesu ankanena za thupi lake lomwe linali ngati kachisi. Patapita zaka zitatu kuchokera pa nthawiyi, ophunzira ake anakumbukira mawu amenewa Yesu ataukitsidwa.

  • Kodi Yesu anapita kuti atachoka ku ukwati wa ku Kana?

  • N’chifukwa chiyani Yesu anakwiya ndi zimene anaona pakachisi, ndipo anachita chiyani?

  • Kodi Yesu ankatanthauza chiyani ponena kuti “kachisi uyu”?

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena