Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • lfb phunziro 18 tsamba 48-tsamba 49 ndime 4
  • Anaona Chitsamba Chikuyaka

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Anaona Chitsamba Chikuyaka
  • Zimene Tingaphunzire Munkhani za M’Baibulo
  • Nkhani Yofanana
  • Chitsamba Choyaka Moto
    Bukhu Langa la Nkhani za Baibulo
  • Mmene Moyo wa Mose Umakukhudzirani
    Galamukani!—2004
  • Chifukwa Chake Mose Akuthawa
    Bukhu Langa la Nkhani za Baibulo
  • Phunzirani Njira za Yehova
    Nsanja ya Olonda—2005
Onani Zambiri
Zimene Tingaphunzire Munkhani za M’Baibulo
lfb phunziro 18 tsamba 48-tsamba 49 ndime 4
Mose ali pafupi ndi chitsamba chomwe chikuyaka

MUTU 18

Anaona Chitsamba Chikuyaka

Mose anakhala ku Midiyani kwa zaka 40. Iye anakwatira n’kukhala ndi ana. Tsiku lina akudyetsa nkhosa pafupi ndi phiri la Sinai, anaona zinthu zodabwitsa. Anaona chitsamba chikuyaka koma sichinkapsa. Atayandikira kuti aone zimene zikuchitika, anamva mawu ochokera m’chitsambacho akuti: ‘Mose! Usayandikire kuno. Vula nsapato zakozo chifukwa malo amene waimawo ndi oyera.’ Yehova ndi amene ankamulankhula ndipo anagwiritsa ntchito mngelo.

Mose anachita mantha kwambiri moti anaphimba nkhope yake. Yehova anamuuza kuti: ‘Ndaona kuti Aisiraeli akuvutika kwambiri. Ndikufuna kuwapulumutsa ku Iguputo n’kuwapititsa kudziko labwino. Iweyo ndi amene uwatsogolere pochoka ku Iguputo.’ Mose ayenera kuti anadabwa kwambiri ndi zimenezi.

Iye anafunsa kuti: ‘Nanga akakandifunsa kuti wakutuma ndi ndani, ndikayankhe kuti chiyani?’ Mulungu anamuuza kuti: ‘Ukawauze kuti, ‘Yehova, Mulungu wa Abulahamu, Mulungu wa Isaki ndi Mulungu wa Yakobo, ndi amene wandituma kwa inu.’ Kenako Mose anati: ‘Nanga akakapanda kundimvera?’ Yehova anapatsa Mose umboni womutsimikizira kuti adzamuthandiza. Yehova anamuuza kuti aponye ndodo yake pansi. Nthawi yomweyo ndodoyo inasanduka njoka. Koma ataigwira kumchira, inasandukanso ndodo. Ndiyeno Yehova anamuuza kuti: ‘Ukakachita zimenezi, akakhulupirira kuti ndakutumadi.’

Koma Mose anati: ‘Pajatu ine ndimavutika kulankhula.’ Ndiyeno Yehova anamulonjeza kuti: ‘Ineyo ndizikakuuza zoyenera kunena ndipo ndikupatsa m’bale wako Aroni kuti azikakuthandiza.’ Mose atadziwa kuti Yehova amuthandiza, anatenga mkazi ndi ana ake n’kuyamba ulendo wopita ku Iguputo.

“Musadzade nkhawa kuti mudzalankhula bwanji kapena kuti mudzanena chiyani, chifukwa zoti mulankhule mudzapatsidwa nthawi yomweyo.”​—Mateyu 10:19

Mafunso: Kodi Mose anaona chiyani akudyetsa nkhosa? Kodi Yehova ankafuna kuti Mose achite chiyani?

Ekisodo 3:1-22; 4:1-20; Machitidwe 7:30-36

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena