Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • lfb phunziro 25 tsamba 64-tsamba 65 ndime 3
  • Chihema Cholambiriramo

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Chihema Cholambiriramo
  • Zimene Tingaphunzire Munkhani za M’Baibulo
  • Nkhani Yofanana
  • Muziyamikira Mwayi Wanu Wolambira M’kachisi Wauzimu wa Yehova
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2023
  • Chihema Cholambirira
    Bukhu Langa la Nkhani za Baibulo
  • ‘Nyumba Yakupemphereramo Anthu a Mitundu Yonse’
    Nsanja ya Olonda—1996
  • Zimene Zili Mʼbuku la Ekisodo
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
Onani Zambiri
Zimene Tingaphunzire Munkhani za M’Baibulo
lfb phunziro 25 tsamba 64-tsamba 65 ndime 3
Chihema ndi bwalo la chihemacho

MUTU 25

Chihema Cholambiriramo

Mose ali kuphiri la Sinai, Yehova anamuuza kuti akonze tenti yapadera yolambiriramo ndipo ankaitchula kuti chihema. Iwo anachikonza m’njira yoti azitha kuchinyamula kulikonse kumene akupita.

Yehova anauza Mose kuti: ‘Uza anthu kuti akupatse zinthu zimene angakwanitse kuti upangire chihema.’ Aisiraeli anapereka golide, siliva, kopa, miyala yamtengo wapatali komanso zodzikongoletsera. Anaperekanso ubweya wa nkhosa, nsalu, zikopa zanyama komanso zinthu zina zambiri. Anthuwo anapereka zinthu zambiri mpaka Mose anachita kuwauza kuti: ‘Basi zakwana. Musabweretsenso zina.’

Aisiraeli abweretsa mphatso zothandizira kumanga chihema

Amuna ndi akazi ambiri aluso anagwira nawo ntchito yomanga chihemachi. Yehova anawapatsa nzeru zowathandiza pogwira ntchitoyi. Ena ankapanga ulusi, kuwomba nsalu komanso kuzikongoletsa. Panalinso ena amene ankapanga zinthu pogwiritsa ntchito miyala, golide kapena mitengo.

Anthuwo anapanga chihema potsatira malangizo amene Yehova anawapatsa. Anapanga katani yokongola imene inagawa Malo Oyera ndi Malo Oyera Koposa. M’Malo Oyera Koposa munali bokosi lotchedwa likasa la pangano. Bokosili linapangidwa ndi golide komanso matabwa a mtengo wa mthethe. M’Malo Oyera munali choikapo nyali chagolide, tebulo ndi guwa lansembe zofukiza. Ndipo pabwalo la chihema panali beseni lakopa ndi guwa lalikulu loperekera nsembe zopsereza. Likasa la pangano linkakumbutsa Aisiraeli kuti analonjeza zoti azimvera Yehova. Kodi ukudziwa kuti pangano n’chiyani? Ndi lonjezo lapadera limene anthu amachita.

Yehova anasankha Aroni ndi ana ake aamuna kuti azigwira ntchito kuchihema n’kumapereka nsembe. Ankayenera kusamalira chihemacho komanso kupereka nsembe kwa Yehova. Aroni yekha, yemwe anali mkulu wa ansembe ndi amene ankaloledwa kulowa m’Malo Oyera Koposa. Iye ankachita zimenezi kamodzi chaka chilichonse pokapereka nsembe ya machimo ake, a banja lake komanso a Aisiraeli onse.

Aisiraeli anamaliza kupanga chihemachi patangotha chaka chimodzi kuchokera pamene anatuluka m’dziko la Iguputo. Apa tsopano anali ndi malo olambirira Yehova.

Ulemerero wa Yehova unadzaza m’chihemacho ndipo mtambo unkakhala pamwamba pake. Mtambowo ukakhala pamwamba pa chihema, Aisiraeli ankakhalabe pamalo omwewo. Koma ukachoka, ankadziwa kuti nthawi yoti anyamuke yakwana. Choncho ankaphwasula chihema chija n’kumatsatira mtambowo ndipo ankakachimanga pamalo ena.

“Kenako ndinamva mawu ofuula kuchokera kumpando wachifumu akuti: ‘Taonani! Chihema cha Mulungu chili pakati pa anthu ndipo iye azidzakhala nawo. Iwo adzakhala anthu ake ndipo Mulunguyo adzakhala nawo.’”​—Chivumbulutso 21:3

Mafunso: Kodi Yehova anauza Mose kuti apange chiyani? Kodi Yehova anapatsa Aroni ndi ana ake udindo wotani?

Ekisodo 25:1-9; 31:1-11; 40:33-38; Aheberi 9:1-7

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena