Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • w93 8/1 tsamba 30
  • Msonkhano wa Pachaka

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Msonkhano wa Pachaka
  • Nsanja ya Olonda—1993
  • Nkhani Yofanana
  • Msonkhano wa Pachaka
    Nsanja ya Olonda—1993
  • Msonkhano Wapachaka—October 3, 1992
    Nsanja ya Olonda—1992
  • Msonkhano Wapachaka—October 3, 1992
    Nsanja ya Olonda—1992
  • Msonkhano Wapachaka—October 5, 1991
    Nsanja ya Olonda—1991
Onani Zambiri
Nsanja ya Olonda—1993
w93 8/1 tsamba 30

Msonkhano wa Pachaka

OCTOBER 2, 1993

MSONKHANO WA PACHAKA wa ziŵalo za Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania udzakhalako pa October 2, 1993, pa Nyumba ya Msonkhano ya Mboni za Yehova, pa 2932 Kennedy Boulevard, Jersey City, ku New Jersey. Msonkhano woyambirira wa ziŵalo zokha udzayamba ndi 9:30 a.m., kenako padzatsatira msonkhano wa pachaka wa onse pa 10:00 a.m.

Ziŵalo za Bungwelo ziyenera kudziŵitsa Ofesi ya Mlembi tsopano za kusintha kulikonse kwa keyala kumene kunachitika mkati mwa chaka chatha kotero kuti makalata anthaŵi zonse achidziŵitso ndi zikalata zotumizira chisankho zikhoza kuwafika msanga pambuyo pa August 1.

Zikalata zotumizira chisankho, zimene zidzatumizidwa kwa ziŵalozo limodzi ndi chidziŵitso cha msonkhano wa pachaka umenewo, ziyenera kubwezeredwa msanga kotero kuti zifike ku Ofesi ya Mlembi wa Sosaite mosachedwera pa August 15. Aliyense amene ali chiŵalo ayenera kudzaza ndi kubwezera chikalata chotumizira chisankho mwamsanga, akunena ngati adzakhalapo pamsonkhano kapena ayi. Zimene alemba pa chikalata chotumizira chisankho ziyenera kumveketsa mfundoyi motsimikizirika, popeza kuti ndizo zidzadaliridwa kudziŵa amene adzapezekapo.

Tikuyembekezera kuti programu yonseyo, kuphatikizapo msonkhano wopenda kagwiridwe ka ntchito ndi malipoti, udzatha pafupifupi ndi 1:00 p.m, kapena kupitirirapo pang’ono. Sipadzakhala gawo la masana. Chifukwa cha kuchepa kwa malo, okhala ndi tikiti okha ndiwo adzaloledwa kuloŵa. Sipadzakhala makonzedwe aliwonse akulunzanitsa msonkhano wa pachaka ndi telefoni ku malo ena osonkhanira.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena