Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • w01 8/1 tsamba 31
  • Mafunso Ochokera kwa Oŵerenga

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Mafunso Ochokera kwa Oŵerenga
  • Nsanja ya Olonda—2001
  • Nkhani Yofanana
  • Yehova Alonjeza Danieli Mphotho Yodabwitsa
    Samalani Ulosi wa Danieli!
  • Mfundo Zazikulu za M’buku la Danieli
    Nsanja ya Olonda—2007
  • Buku la Danieli ndi Inu
    Samalani Ulosi wa Danieli!
  • Ayesedwa—Koma Akhulupirikabe kwa Yehova!
    Samalani Ulosi wa Danieli!
Onani Zambiri
Nsanja ya Olonda—2001
w01 8/1 tsamba 31

Mafunso Ochokera kwa Oŵerenga

Kodi Danieli anali kuti pamene Ahebri atatu aja anawayesa kuti alambire fano lalikulu limene Nebukadinezara anaimika m’chigwa cha Dura?

Baibulo silimanena, motero palibe munthu lerolino amene angadziŵe kumene Danieli anali panthaŵi ya kuyesedwako.

Ena anena kuti udindo wa Danieli m’boma kapena mphamvu zapadera zimene Nebukadinezara anam’patsa zinali zapamwamba kuposa za Sadrake, Mesake, ndi Abedinego ndipo motero sanafunike kupita ku chigwa cha Dura. Danieli 2:49 amanenadi kuti nthaŵi ina iye anali ndi udindo wapamwamba kuposa anzake atatuwo. Koma palibe umboni wakuti zimenezi zinam’chititsa kuti asapezeke nawo pa kulambira fanoli.

Poyesa kufotokoza chifukwa chake Danieli sanapezekepo, ena anena kuti mwina anapita kwina kukagwira ntchito za boma kapena anadwala motero analephera kupezekapo. Komabe, Baibulo silinena zimenezo. Mulimonse mmene zinalili, zimene Danieli anachita ziyenera kuti sizinali zoti angampeze nazo chifukwa. Zikanakhala zotero, mosakayika nduna za boma za nsanje zikanagwiritsa ntchito kusapezekapo kwakeko kukhala chifukwa chomuimbira mlandu. (Danieli 3:8) Zimenezi zisanachitike ndiponso pambuyo pake, Danieli anasunga umphumphu ndipo anakhulupirika kwa Mulungu ngakhale kuti anakumana ndi mayesero ambiri. (Danieli 1:8; 5:17; 6:4, 10, 11) Choncho, ngakhale kuti Baibulo silinena chifukwa chake Danieli sanapezeke ku chigwa cha Dura, tingakhulupirire kuti anakhulupirikabe kwa Yehova Mulungu mosagonja.​—Ezekieli 14:14; Ahebri 11:33.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena