Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • w05 9/15 tsamba 3
  • Kodi Anali Mulungu Kapena Munthu?

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Kodi Anali Mulungu Kapena Munthu?
  • Nsanja ya Olonda—2005
  • Nkhani Yofanana
  • Fufuzani Chuma Chimene ‘Chinabisidwa Mosamala mwa Iye’
    Nsanja ya Olonda—2009
  • Tsatirani Kuunika kwa Dziko
    Nsanja ya Olonda—1993
  • Munthu Wamkulu Woposa Onse Amene Anakhalako
    Nsanja ya Olonda—1992
  • Yesu Kristu—Kodi Anatumidwa ndi Mulungu?
    Mungathe Kukhala ndi Moyo Kosatha m’Paradaiso pa Dziko Lapansi
Onani Zambiri
Nsanja ya Olonda—2005
w05 9/15 tsamba 3

Kodi Anali Mulungu Kapena Munthu?

“INE ndine kuunika kwa dziko lapansi; iye wonditsata Ine sadzayenda mumdima, koma adzakhala nako kuunika kwa moyo.” (Yohane 8:12) Yesu Kristu ndiye ananena mawu amenewa. Munthu wina wophunzira wa m’zaka 100 zoyambirira analemba za Yesu kuti: “Zolemera zonse za nzeru ndi chidziwitso zibisika mwa Iye.” (Akolose 2:3) Kuphatikizanso apo, Baibulo limati: “Moyo wosatha ndi uwu, kuti akadziwe Inu Mulungu woona yekha, ndi Yesu Kristu amene munam’tuma.” (Yohane 17:3) Kuti tikhale osangalala mwauzimu timafunikira kudziwa zenizeni zokhudza Yesu.

Padziko lonse anthu ambiri anamvapo ndithu za Yesu Kristu. N’zosachita kufunsa kuti iye anakhudza kwabasi mbiri ya anthu. Ngakhale kawerengedwe ka madeti pa kalendala imene madera ambiri a padziko lonse amagwiritsira ntchito kamayambira pa chaka chimene akuti Yesu anabadwa. Buku la The World Book Encyclopedia limati: “Madeti a zinthu zimene zinachitika chaka chimenechi chisanakwane, anthu ambiri amawatchula kuti B.C., kapena kuti Kristu asanabadwe. Ndipo madeti a zinthu zimene zinachitika chaka chimenechi chitakwana amawatchula kuti A.D. kapena kuti m’chaka cha Ambuye wathu.”

Komabe, anthu sagwirizana chimodzi pa nkhani yakuti Yesu anali ndani makamaka. Kwa ena, iye anali munthu wotchuka basi, amene ndi wodziwika m’mbiri ya anthu. Koma ena amamulambira ngati Mulungu Wamphamvuyonse. Ahindu ena amayerekezera Yesu Kristu ndi mulungu wa Chihindu wotchedwa Krishna, amene ambiri amati ndi mulungu wovala thupi la munthu. Kodi Yesu anali munthu ngati wina aliyense, kapena kodi anali woyenera kumulambira? Kodi anali ndani makamaka? Anachokera kuti? Kodi anali wotani? Nanga panopo ali kuti? Monga tionere m’nkhani yotsatirayi, buku limene limanena zinthu zambiri zokhudza Yesu, lili ndi mayankho oona a mafunso amenewa.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena