Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • w07 9/15 tsamba 3
  • N’chifukwa Chiyani Mulungu Walola Kuti Zoipa Zizichitika?

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • N’chifukwa Chiyani Mulungu Walola Kuti Zoipa Zizichitika?
  • Nsanja ya Olonda—2007
  • Nkhani Yofanana
  • Chabwino Motsutsana ndi Choipa—Nkhondo Yakalekale
    Nsanja ya Olonda—1993
  • Kodi Chabwino Chidzagonjetsadi Choipa?
    Nsanja ya Olonda—1993
  • Ncifukwa Ninji Mulungu Wakulola Kuipa Kupitirizabe Mpaka Lero?
    Coonadi Cimene Cimatsogolera ku Moyo Wamuyaya
  • N’chifukwa Chiyani Mulungu Amalola Kuti Tizivutika?
    Galamukani!—2004
Onani Zambiri
Nsanja ya Olonda—2007
w07 9/15 tsamba 3

N’chifukwa Chiyani Mulungu Walola Kuti Zoipa Zizichitika?

SIMUNGACHITE kuyenda mtunda wautali kuti muone zinthu zoipa kapena anthu akuvutika. Asilikali ngakhalenso anthu wamba amafa pa nkhondo. Chiwawa ndi umbanda zili paliponse. Mwina inu mwavutikapo chifukwa cha tsankho ndi kupanda chilungamo. Chifukwa cha zimene mwaona ndi kukumana nazo, muyenera kuti munafunsapo kuti: ‘N’chifukwa chiyani Mulungu walola kuti zoipa zizichitika?’

Anthu sanayambe lero kufunsa funso limeneli. Zaka pafupifupi 3,600 zapitazo, Yobu yemwe anali mtumiki wokhulupirika wa Mulungu, anafunsa kuti: “Oipa akhaliranji ndi moyo?” (Yobu 21:7) Ndiponso zaka pafupifupi 2,600 zapitazo, mneneri Yeremiya, chifukwa chokhumudwa kwambiri ndi zochita za anthu m’dziko lake, anafunsa kuti: “Chifukwa chanji ipindula njira ya oipa? Chifukwa chanji akhala bwino onyengetsa?” (Yeremiya 12:1) Yobu ndi Yeremiya ankadziwa kuti Mulungu ndi wolungama. Koma onsewa anafuna kudziwa chifukwa chake padziko pali zoipa zambiri chonchi. Mwina nanunso zimenezi zimakudabwitsani.

Anthu ena amaganiza kuti Mulungu ndi amene amachititsa zoipa ndiponso kuvutika kwa anthu. Ena amadzifunsa kuti: ‘Ngati Mulungu ali wamphamvu yonse, wolungama ndiponso wachikondi, kodi n’chifukwa chiyani sakuthetsa zoipa ndi kuvutika? N’chifukwa chiyani walola kuti zoipa zizichitika mpaka pano?’ Nkhani yotsatirayi iyankha mafunso amenewa ndiponso mafunso ena ofunika kwambiri.

[Mawu a Chithunzi patsamba 3]

AP Photo/​Adam Butler

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena