Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • w12 12/1 tsamba 3
  • Zimene Ena Amachita pa Khirisimasi Pofuna Kusangalala

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Zimene Ena Amachita pa Khirisimasi Pofuna Kusangalala
  • Nsanja ya Olonda—2012
  • Nkhani Yofanana
  • N’chifukwa Chiyani a Mboni za Yehova Sakondwerera Khirisimasi?
    Mafunso Ofunsidwa Kawirikawiri
  • Kodi Krisimasi Imatanthauzanji kwa Inu?
    Nsanja ya Olonda—1994
  • Chiyambi cha Krisimasi Yamakono
    Nsanja ya Olonda—1997
  • Kodi Nkhani Yaikulu Panyengo ya Khirisimasi Imakhala Chiyani?
    Nsanja ya Olonda—2005
Onani Zambiri
Nsanja ya Olonda—2012
w12 12/1 tsamba 3

Zimene Ena Amachita pa Khirisimasi Pofuna Kusangalala

“N’zosavuta kutengeka ndi zimene anthu amachita pa nthawi ya Khirisimasi. Komabe pa nthawi ya holide ngati imeneyi pamakhala zambiri zochita moti anthu sakhalanso ndi nthawi yokwanira yocheza ndi achibale komanso anzawo. Choncho m’malo moti tisangalale pa nthawiyi, timakhala otanganidwa kwambiri ndipo zimangotiwonjezera mavuto.”—BRAD HENRY, BWANAMKUBWA WAKALE WA KU OKLAHOMA [U.S.A.] ANANENA ZIMENEZI PA DECEMBER 23, 2008.

NTHAWI ya Khirisimasi ikamayandikira pamakhala nyimbo, mafilimu komanso mapulogalamu a pa TV zimene zimapangitsa anthu kuona kuti nthawiyi ndi yosangalatsa. Kodi mukuganiza kuti chinthu chofunika kwambiri kuchita pa Khirisimasi n’chiyani? Kapena kodi ndi

  • Kukumbukira Yesu Khristu?

  • Kupatsana mphatso?

  • Kuthandiza osowa?

  • Kukachezera achibale?

  • Kukhala mwamtendere?

Monga mmene mawu a bwanamkubwa amene ali kumanzerewa akusonyezera, anthu ambiri amalephera kuchita zimene ankafuna pa nthawi ya Khirisimasi. Pa nthawiyi anthu ambiri amakhala otanganidwa kwambiri, ankhawa komanso amawononga ndalama zambiri kugula zinthu. Koma kodi zimenezi zikutanthauza kuti anthu sangapeze zochita zina mkati mwa chaka zimene zingachititse kuti azikhala osangalala?

Baibulo limatilimbikitsa kuti tiyenera kukumbukira Yesu Khristu, kukhala owolowa manja, kuthandiza osowa komanso kuchezera achibale. Komanso limatiphunzitsa kuti tiyenera kukhala amtendere. Choncho m’malo mokambirana chifukwa chimene anthu ena sakondwerera Khirisimasi,a m’nkhanizi tikambirana mafunso otsatirawa:

  • Kodi n’chifukwa chiyani anthu ambiri amaona kuti n’koyenera kukondwerera Khirisimasi?

  • Kodi n’chiyani chimachititsa kuti anthu asamasangalale pa nthawi ya Khirisimasi ngati mmene amafunira?

  • Ndi mfundo ziti za m’Baibulo zimene zathandiza anthu ambiri kukhala osangalala ngakhale kuti sakondwerera Khirisimasi?

a Kuti mudziwe mfundo za m’Malemba zimene zimapangitsa anthu ena kuti asamachite Khirisimasi, onani nkhani yakuti, “Zimene Owerenga Amafunsa—N’chifukwa Chiyani Anthu Ena Sachita Nawo Khirisimasi?”

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena