Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • w13 2/1 tsamba 16
  • Kuyankha Mafunso a M’Baibulo

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Kuyankha Mafunso a M’Baibulo
  • Nsanja ya Olonda—2013
  • Nkhani Yofanana
  • Kodi Mulungu Analenga Mdyerekezi?
    Kuyankha Mafunso a M’Baibulo
  • Mdani wa Moyo Wosatha
    Mungathe Kukhala ndi Moyo Kosatha m’Paradaiso pa Dziko Lapansi
  • Kodi Baibulo Limanena Zotani?
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yogawira)—2016
  • “Tsutsani Mdyerekezi” Monga Anachitira Yesu
    Nsanja ya Olonda—2008
Onani Zambiri
Nsanja ya Olonda—2013
w13 2/1 tsamba 16

KUYANKHA MAFUNSO A M’BAIBULO

Kodi Mdyerekezi anachokera kuti?

Mulungu sanalenge Mdyerekezi, koma analenga mngelo wabwinobwino yemwe kenako anachita zinthu zomwe zinachititsa kuti akhale Mdyerekezi kapena kuti Satana. Yesu anasonyeza kuti poyamba Mdyerekezi anali mngelo wolungama ndipo anali mmodzi mwa ana a Mulungu.—Werengani Yohane 8:44.

Kodi zinatheka bwanji kuti mngelo wabwinobwino akhale Mdyerekezi?

Mngelo amene anakhala Mdyerekezi anapandukira Mulungu ndipo anachititsanso anthu oyambirira kupandukira Mulungu. Choncho iye anadzichititsa kukhala Satana kutanthauza “Wotsutsa.”—Werengani Genesis 3:1-5; Chivumbulutso 12:9.

Mofanana ndi anthu komanso angelo onse, mngelo amene anakhala Mdyerekezi anali ndi ufulu wosankha kuchita zabwino kapena zoipa, koma iye anayamba kufuna kuti azilambiridwa. Iye ankafuna kwambiri kuti azilambiridwa kuposa kukondweretsa Mulungu.—Werengani Mateyu 4:8, 9; Yakobo 1:13, 14.

Kodi Mdyerekezi akupitirizabe kusocheretsa anthu pogwiritsa ntchito njira ziti? Kodi tiyenera kumuopa? Mungapeze mayankho a mafunso amenewa m’Baibulo.

Mayankho a mafunso ena a m’Baibulo mungawapeze pa Webusaiti yathu

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena