Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • w13 7/15 tsamba 32
  • “Zithunzi Zokongola Kwambiri”

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • “Zithunzi Zokongola Kwambiri”
  • Nsanja ya Olonda—2013
  • Nkhani Yofanana
  • Oyang’anira Amene Amatitsogolera—Wochititsa Phunziro la Nsanja ya Olonda
    Utumiki Wathu wa Ufumu—1998
  • Phunziro Labuku Lampingo Limachirikiza Zochita Zophunzitsa
    Utumiki Wathu wa Ufumu—1994
  • Gwiritsani Chilengezo Chapoyera cha hiyembekezo Chanu Mosagwedera
    Utumiki Wathu wa Ufumu—1994
  • Tizilimbikitsana Pamisonkhano ya Mpingo
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2023
Onani Zambiri
Nsanja ya Olonda—2013
w13 7/15 tsamba 32

“Zithunzi Zokongola Kwambiri”

Mwina inuyo mutatsegula magazini yatsopano, munaonapo kuti zinthunzi zake n’zokongola kwambiri. Pamakhala chintchito kuti zithunzi zokongola zimenezi zijambulidwe ndipo zimakhala ndi cholinga chapadera. Zimathandiza kuti nkhanizo zitifike pa mtima ndiponso tiziganizire kwambiri. Zithunzi zingathandize kwambiri pokonzekera ndiponso poyankha pa Phunziro la Nsanja ya Olonda.

Mwachitsanzo, mungachite bwino kuganizira chithunzi chimene chimakhala kumayambiriro kwa nkhani yophunzira. Muzidzifunsa kuti, N’chifukwa chiyani anaika chithunzi chimenechi? Kodi chikusonyeza chiyani? Nanga chikugwirizana bwanji ndi mutu wa nkhani kapena lemba loyambirira? Mungachitenso bwino kuganizira zithunzi zina ndiponso kuona kugwirizana kwake ndi nkhaniyo komanso zochitika pa moyo wanu.

M’bale amene akuchititsa Phunziro la Nsanja ya Olonda ayenera kupereka mpata kwa abale ndi alongo kuti afotokoze chithunzi chilichonse. Iwo afotokoze kugwirizana kwake ndi nkhaniyo komanso mmene chithunzicho chawathandizira. Nthawi zina, pachithunzi pamakhala mawu osonyeza ndime imene ikugwirizana nacho. Koma nthawi zina wochititsa amafunika kuona yekha kuti ndi pandime iti pamene angakambirane chithunzi. Kuchita zimenezi kungathandize kuti aliyense athandizidwe ndi zithunzi zomwe zajambulidwa n’cholinga choti timvetse bwino Mawu a Mulungu.

M’bale wina anati: “Nkhani zimalembedwa bwino koma zithunzi zimakometsera nkhanizo kuti zikhale zogwira mtima kwambiri.”

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena