Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • w13 11/1 tsamba 16
  • Kuyankha Mafunso a M’Baibulo

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Kuyankha Mafunso a M’Baibulo
  • Nsanja ya Olonda—2013
  • Nkhani Yofanana
  • Kodi Ndani Amene Amapita Kumwanba, ndipo Nchifukwa Ninji?
    Mungathe Kukhala ndi Moyo Kosatha m’Paradaiso pa Dziko Lapansi
  • Kuyankha Mafunso a M’Baibulo
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova—2015
  • Kodi Akhristu Onse Okhulupirika Amapita Kumwamba?
    Nsanja ya Olonda—2011
  • Kodi Anthu Onse Abwino Amapita Kumwamba?
    Nsanja ya Olonda—2010
Onani Zambiri
Nsanja ya Olonda—2013
w13 11/1 tsamba 16
[Chithunzi patsamba 16]

KUYANKHA MAFUNSO A M’BAIBULO

Kodi ndani amapita kumwamba ndipo n’chifukwa chiyani?

Anthu ambiri amanena kuti adzapita kumwamba akadzamwalira. Yesu ananena kuti atumwi ake okhulupirika adzapita kumwamba. Asanamwalire, anawalonjeza kuti akupita kumwamba kwa Atate ake kukawakonzera malo.—Werengani Yohane 14:2.

N’chifukwa chiyani anthu ena amaukitsidwa kuti apite kumwamba? Kodi amapita kukatani? Yesu anauza atumwi ake kuti adzakhala mafumu ndipo adzalamulira dziko lapansi.—Werengani Luka 22:28-30; Chivumbulutso 5:10.

Kodi anthu onse abwino amapita kumwamba?

M’mayiko ambiri, anthu ochepa okha ndi amene amakhala olamulira. Popeza Yesu amaukitsa anthu kuti akakhale mafumu kumwamba, tikuyembekezera kuti anthu amene adzalamulira dziko lapansi ayenera kukhalanso ochepa. (Luka 12:32) Baibulo limatchula nambala yeniyeni ya anthu amene adzalamulire ndi Yesu kumwamba.—Werengani Chivumbulutso 14:1.

Yesu anakonzera otsatira ake ena malo kumwamba. Kodi mukudziwa zimene azidzachita kumwambako?

Komatu si anthu okhawa amene adzalandire mphoto ya moyo wosatha. Anthu amene adzakhale nzika za Ufumu wa Mulungu adzasangalala ndi moyo wosatha m’Paradaiso padziko lapansi. (Yohane 3:16) Anthu ena adzapulumuka n’kulowa m’Paradaiso Mulungu akamadzawononga anthu oipa, pamene ena adzachita kuukitsidwa kuchokera kumanda.—Werengani Salimo 37:29; Yohane 5:28, 29.

Kuti mudziwe zambiri, werengani mutu 8 m’buku ili, Kodi Baibulo Limaphunzitsa Chiyani Kwenikweni? lomwe ndi lofalitsidwa ndi Mboni za Yehova

Mungachitenso dawunilodi bukuli pa www.jw.org

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena