Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • w15 11/1 tsamba 16
  • Kuyankha Mafunso a M’Baibulo

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Kuyankha Mafunso a M’Baibulo
  • Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova—2015
  • Nkhani Yofanana
  • Kuyankha Mafunso a M’Baibulo
    Nsanja ya Olonda—2013
  • Kuyankha Mafunso a M’Baibulo
    Nsanja ya Olonda—2013
  • Anthu Amene Anamwalira Adzakhalanso ndi Moyo
    Zimene Baibulo Limaphunzitsa
  • Kodi Mawu Akuti Kuuka kwa Akufa Amatanthauza Chiyani?
    Kuyankha Mafunso a M’Baibulo
Onani Zambiri
Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova—2015
w15 11/1 tsamba 16

KUYANKHA MAFUNSO A M’BAIBULO

Kodi akufa adzakhalanso ndi moyo?

Anthu akusangalala kwambiri kukumananso ndi abale awo omwe anamwalira

N’zomveka kuti Mulungu adzaukitsa anthu chifukwa ndi amene anatilenga

Yehova Mulungu ndi amene analenga zinthu zonse. (Salimo 36:9) Popeza ndi amene analenga zonse, n’zosakayikitsa kuti adzaukitsa anthu omwe anamwalira. (Werengani Machitidwe 24:15) Koma n’chifukwa chiyani adzachite zimenezi?

Pamene Mulungu ankalenga anthu sankafuna kuti azifa. (Genesis 1:31; 2:15-17) Iye sanasinthe maganizo akewa ndipo amafunabe kuti anthu adzakhale ndi moyo padzikoli mpaka kalekale. Choncho zimamupweteka kwambiri akamaona anthu akuvutika kenako n’kufa.—Werengani Yobu 14:1, 14, 15.

Kodi anthu oukitsidwa adzakhala kuti?

Kodi Mulungu analenga anthu kuti azikhala kuti? Anawalenga kuti azikhala padziko lapansi. Koma angelo ndi amene anawalenga kuti azikhala kumwamba. (Genesis 1:28; Yobu 38:4, 7) Komanso kumbukirani kuti Yesu ali padziko lapansi anaukitsa anthu ndipo anthuwo anakhala padziko lapansi lomweli. Ndi zimenenso zidzachitike mtsogolomu. Anthu ambiri omwe adzaukitsidwe azidzakhala padziko lapansili.—Werengani Yohane 5:28, 29; 11:44.

Koma pali anthu ena ochepa omwe Mulungu wasankha kuti adzaukitsidwire kumwamba. Anthuwa adzaukitsidwa ndi matupi ngati a angelo. (Luka 12:32; 1 Akorinto 15:49, 50) Anthu amenewa adzakhala mafumu limodzi ndi Khristu kumwamba ndipo azidzalamulira dziko lapansili.—Werengani Chivumbulutso 5:9, 10.

Kuti mudziwe zambiri, werengani mutu 7 m’buku lakuti Kodi Baibulo Limaphunzitsa Chiyani Kwenikweni? lofalitsidwa ndi a Mboni za Yehova

Bukuli likupezekanso pa webusaiti yathu ya www.jw.org/ny

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena