Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • w14 1/1 tsamba 16
  • Kuyankha Mafunso a M’Baibulo

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Kuyankha Mafunso a M’Baibulo
  • Nsanja ya Olonda—2014
  • Nkhani Yofanana
  • Kodi Zinthu Zopanda Chilungamo Zidzatha Padzikoli?
    Nkhani Zina
  • N’zotheka Kupirira Zinthu Zopanda Chilungamo
    Nsanja ya Olonda—2007
  • Kodi Mulungu Adzachitapodi Kanthu Ponena za Chisalungamo?
    Nsanja ya Olonda—1989
  • “Kodi Mulungu Alibe Chilungamo?”
    Yandikirani Yehova
Onani Zambiri
Nsanja ya Olonda—2014
w14 1/1 tsamba 16
Mayi ndi mwana, omwe ali pa umphawi wadzaoneni

KUYANKHA MAFUNSO A M’BAIBULO

Kodi Mulungu ndi wotani?

Sitingathe kuona Mulungu chifukwa iye ndi mzimu. Mulungu ndi amene analenga kumwamba, dziko lapansili komanso zinthu zonse zamoyo. Mulungu sanachite kulengedwa ndipo alibe chiyambi. (Salimo 90:2) Mulungu amafuna kuti anthu adziwe zoti iye alipo komanso kuti adziwe zolondola zokhudza iyeyo.—Werengani Machitidwe 17:24-27.

Tiyeneranso kudziwa kuti Mulungu ali ndi dzina. Tingathe kudziwa makhalidwe ake poona zinthu zimene iye analenga. (Aroma 1:20) Koma kuti timudziwe bwino, tiyenera kuphunzira Baibulo, lomwe ndi Mawu ake. Baibulo limatithandiza kudziwa kuti Mulungu ndi wachikondi.—Werengani Salimo 103:7-10.

Kodi Mulungu amamva bwanji zinthu zopanda chilungamo zikamachitika?

Mlengi wathu, Yehova, amadana ndi kupanda chilungamo ndipo iye analenga anthufe m’chifaniziro chake. (Deuteronomo 25:16) N’chifukwa chake ambirife timadananso ndi zachinyengo. Zinthu zopanda chilungamo zimene zimachitikazi, si Mulungu amene amazichititsa. Mulungu anapatsa anthu ufulu wosankha. Koma n’zomvetsa chisoni kuti anthu ambiri amagwiritsa ntchito molakwika ufulu umenewu ndipo amachita zinthu zopanda chilungamo. Zimenezi zimakhumudwitsa kwambiri Yehova.—Werengani Genesis 6:5, 6; Deuteronomo 32:4, 5.

Yehova amakonda chilungamo ndipo sadzalola kuti zinthu zopanda chilungamo zipitirire kuchitika mpaka kalekale. (Salimo 37:28, 29) Baibulo limalonjeza kuti, posachedwapa Mulungu adzathetsa zinthu zonse zopanda chilungamo.—Werengani 2 Petulo 3:7-9, 13.

Baibulo limalonjeza kuti posachedwapa Mulungu adzathetsa zinthu zonse zopanda chilungamo

Kuti mudziwe zambiri, werengani mutu 1 m’buku lakuti Kodi Baibulo Limaphunzitsa Chiyani Kwenikweni? lofalitsidwa ndi Mboni za Yehova.

Bukuli likupezekanso pa webusaiti yathu ya www.jw.org

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena