Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • w14 8/1 tsamba 5
  • Mulungu Amakumvetsani

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Mulungu Amakumvetsani
  • Nsanja ya Olonda—2014
  • Nkhani Yofanana
  • Yehova Amatidziŵa Bwino!
    Nsanja ya Olonda​—1990
  • Kodi Mulungu Amakudziŵanidi?
    Nsanja ya Olonda—1993
  • Kodi Mulungu Amakumvetsani?
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yogawira)——2018
  • Tinapangidwa Modabwitsa Kwambiri
    Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Ndandanda ya Misonkhano—2016
Onani Zambiri
Nsanja ya Olonda—2014
w14 8/1 tsamba 5

NKHANI YA PACHIKUTO | KODI MULUNGU AMAKUONANI KUTI NDINU WOFUNIKA?

Mulungu Amakumvetsani

“Inu Yehova, mwandifufuza ndipo mukundidziwa.”—SALIMO 139:1.

DNA ndi kamwana kosabadwa

“Maso anu anandiona pamene ndinali mluza.” —SALIMO 139:16

N’CHIFUKWA CHIYANI ANTHU ENA AMAKAYIKIRA? Anthu ambiri amaganiza kuti Mulungu amangoona kuti anthu ndi ochimwa komanso odetsedwa ndipo alibe nawo ntchito. Mtsikana wina dzina lake Kendra, yemwe ankadwala matenda a maganizo, ankangokhalira kudziimba mlandu chifukwa ankaona kuti amalephera kuchita zonse zimene Mulungu amafuna. Iye ananena kuti zimenezi zinachititsa kuti asiye kupemphera.

ZIMENE BAIBULO LIMANENA: Sikuti Yehova amangoona zimene mumalakwitsa. Iye amaonanso zimene zili mumtima mwanu ndipo amakumvetsani. Baibulo limanena kuti: “Akudziwa bwino mmene anatiumbira, amakumbukira kuti ndife fumbi.” Komanso ‘satichitira mogwirizana ndi machimo athu,’ koma amatikhululukira tikalapa.—Salimo 103:10, 14.

Taganizirani zimene zinachitikira Davide yemwe anali mfumu ya Aisiraeli. Iye anapemphera kuti: “Maso anu anandiona pamene ndinali mluza, ndipo ziwalo zanga zonse zinalembedwa m’buku lanu. . . . Ndifufuzeni, inu Mulungu, ndi kudziwa mtima wanga.” (Salimo 139:16, 23) Davide ankadziwa kuti ngakhale kuti pa nthawi ina anachitapo machimo akuluakulu, koma atalapa kuchokera pansi pa mtima, Yehova anazindikira zimenezi ndipo anamukhululukira.

Dziwani kuti Yehova amakumvetsani kuposa munthu wina aliyense. Baibulo limati: “Munthu amaona zooneka ndi maso, koma Yehova amaona mmene mtima ulili.” (1 Samueli 16:7) Mulungu amadziwa zimene zimakupangitsani kuti muzichita zinazake. Kaya ndi chifukwa cha chibadwa chanu, mmene munaleredwera kapenanso kumene mukukhala, Mulungu amamvetsa zonsezo. Ngati mukuyesetsa kuti muzichita zabwino, iye amaona komanso amasangalala ngakhale kuti mumalakwitsa zinthu zina.

Popeza Mulungu amakumvetsani chonchi, kodi amakuthandizani bwanji pogwiritsa ntchito zomwe amadziwazo?

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena