Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • wp17 No. 5 tsamba 16
  • Kodi Baibulo Limanena Zotani?

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Kodi Baibulo Limanena Zotani?
  • Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yogawira)—2017
  • Timitu
  • Nkhani Yofanana
  • Kodi padzikoli padzakhaladi mtendere?
  • Kodi n’zotheka panopa kukhala ndi mtendere wamumtima?
  • Mtendere Weniweni—Kodi Udzachokera Kuti?
    Nsanja ya Olonda—1997
  • Kodi N’zotheka Kukhala ndi Mtendere M’dziko la Mavutoli?
    Nsanja ya Olonda—2009
  • Kodi Adzatsogolera Anthu ku Mtendere Ndani?
    Nsanja ya Olonda​—1990
  • Lolani “Mtendere wa Mulungu” Uchinjirize Mtima Wanu
    Nsanja ya Olonda—1991
Onani Zambiri
Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yogawira)—2017
wp17 No. 5 tsamba 16
Zida zonse zankhondo zikuwonongedwa

Zida zonse zankhondo zidzawonongedwa

Kodi Baibulo Limanena Zotani?

Kodi padzikoli padzakhaladi mtendere?

Kodi mungayankhe bwanji?

  • Inde

  • Ayi

  • Mwina

Zimene Baibulo limanena

Yesu Khristu akadzayamba kulamulira padzikoli, “padzakhala mtendere wochuluka kwa nthawi yonse pamene mwezi udzakhalepo.” Izi zikutanthauza kuti mtenderewo udzakhalapo mpaka kalekale.​—Salimo 72:7.

Mfundo zinanso zomwe tikuphunzira m’Baibulo

  • Anthu onse oipa adzawonongedwa. Zimenezi zidzachititsa kuti anthu abwino ‘adzasangalale ndi mtendere wochuluka.’​—Salimo 37:10, 11.

  • Mulungu adzathetsa nkhondo padziko lonse.​—Salimo 46:8, 9.

Kodi n’zotheka panopa kukhala ndi mtendere wamumtima?

Anthu ena amakhulupirira kuti . . . n’zosatheka kukhala ndi mtendere wamumtima panopa chifukwa padzikoli pali mavuto ambiri komanso pakuchitika zinthu zopanda chilungamo. Kodi inuyo mukuganiza bwanji?

Zimene Baibulo limanena

Ngakhale panopa, anthu amene ali pa ubwenzi wolimba ndi Mulungu akhoza kukhala ndi “mtendere wa Mulungu umene umaposa kuganiza mozama kulikonse.”​—Afilipi 4:6, 7.

Mfundo zinanso zomwe tikuphunzira m’Baibulo

  • Mulungu akulonjeza kuti adzathetsa mavuto onse komanso zinthu zopanda chilungamo, ndipo ‘adzapanga zinthu zonse kukhala zatsopano.’​—Chivumbulutso 21:4, 5.

  • Tikhoza kukhala ndi mtendere wamumtima ngati timayesetsa kupeza ‘zosowa zathu zauzimu.’—Mateyu 5:3.

Kuti mudziwe zambiri, werengani mutu 3 m’buku ili, Zimene Baibulo Limaphunzitsa, lofalitsidwa ndi a Mboni za Yehova

Bukuli likupezekanso pawebusaiti yathu ya www.jw.org/ny

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena