Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • km 2/02 tsamba 7
  • Bokosi la Mafunso

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Bokosi la Mafunso
  • Utumiki wathu wa Ufumu—2002
  • Nkhani Yofanana
  • Kuyesetsa Kuti Anthu Mumpingo Apitirize Kukhala Amtendere Komanso Oyera
    Gulu Lochita Chifuniro cha Mulungu
  • Mmene Bungwe Lolamulira Limayendetsera Ntchito Zake
    Nsanja ya Olonda—2008
  • Akulu, Weruzani Mwachilungamo
    Nsanja ya Olonda—1992
  • Oyang’anira Amene Amaweta Nkhosa za Mulungu
    Gulu Lochita Chifuniro cha Mulungu
Utumiki wathu wa Ufumu—2002
km 2/02 tsamba 7

Bokosi la Mafunso

◼ Kodi komiti ya chiweruzo ya mpingo itatha kumvetsera nkhani ya munthu wolakwa ndi kupenda umboni wonse wa nkhaniyo ndi kugamula kuti munthu wolakwayo achotsedwe mu mpingo, kodi azitani naye?

Ndibwino kuti komiti ya chiweruzo ilankhule naye munthuyo, kumuuza kuti komitiyo yagamula kuti achotsedwe mumpingo. Ndiyeno imufunse ngati akufuna kuchita apilo. Angachite apilo ngati akuona kuti komitiyo sinagamule bwino nkhaniyo. Panthaŵi imene akufuna kuchita apilo, komitiyo isalengeze zimene yagamulazo. Zikatere amuuze kuti achite apiloyo pasanathe mlungu umodzi. Achite zimenezi mwa kulembera kalata komiti ya chiweruzo, ndipo apereke zifukwa zake. Komiti ya chiweruzo ikalandira kalatayo, tcheyamani wa komitiyo alankhule mwachangu ndi woyang’anira dera, amene kenako adzasankhe akulu oti aimire komiti ya apilo.

Pakatha mlungu umodzi asanachite apiloyo, lengezani kumpingo kuti wachotsedwa. Komiti ya chiweruzo izilemba chilengezo chokaŵerenga ku mpingo. Woyang’anira wotsogolera apende chilengezocho kuti aone ngati chikugwirizana ndi malangizo a Bungwe Lolamulira. Zikatero, mkulu, kapena tcheyamani wa komiti ya chiweruzo, aŵerenge chilengezocho ku mpingo pa Msonkhano wa Utumiki wotsatira.

Komanso, akulu a m’komiti ya chiweruzo am’fotokozere munthu wolakwayo kufunika kolapa ndiponso zina zimene angachite kuti panthaŵi yake adzabwezeretsedwe. Izi n’zothandiza ndiponso zabwino, pamene tikuyembekeza kuti adzasinthe njira zake ndi kubwerera m’gulu la Yehova m’kupita kwa nthaŵi.—2 Akor. 2:6, 7.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena