Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • km 3/99 tsamba 1
  • Aitaneni Kuti Afike

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Aitaneni Kuti Afike
  • Utumiki Wathu wa Ufumu—1999
  • Nkhani Yofanana
  • Makhalidwe Amene Amatichititsa Kupezeka Pamisonkhano
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2019
  • Kodi Misonkhano ya Mboni za Yehova Ingakuthandizeni Bwanji?
    Mungakhale Ndi Moyo Mpaka Kalekale—Kuphunzira Baibulo Mokambirana
  • “Mzimu ndi Mkwatibwi Akunenabe Kuti: ‘Bwera!’”
    Nsanja ya Olonda—2010
  • N’chifukwa Chiyani Tiyenera Kusonkhana?
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2016
Onani Zambiri
Utumiki Wathu wa Ufumu—1999
km 3/99 tsamba 1

Aitaneni Kuti Afike

1 Chiitano choperekedwa zaka mazana apitawo tsopano chikuperekedwa m’mayiko 233 padziko lonse chakuti: “Tiyeni tikwere kunka ku phiri la Yehova, . . . ndipo Iye adzatiphunzitsa za njira zake, ndipo tidzayenda m’mayendedwe ake.” (Yes. 2:3) Kusonyeza anthu gulu la Yehova ndi imodzi mwa njira zabwino kwambiri zimene tingathandizire anthu kupita patsogolo mwauzimu komwe kumatsogolera kumoyo wosatha.

2 Ofalitsa ena amachedwa kuitanira anthu ku Nyumba ya Ufumu mpaka ataona kuti afika patali paphunziro lawo la Baibulo lapanyumba. Komabe, nthaŵi zina anthu amayamba kumafika pamisonkhano ya mpingo ngakhale asanayambitsidwe phunziro la Baibulo. Tisachedwe kupereka chiitano kwa anthu ndi kuwalimbikitsa kufika pamisonkhano.

3 Zoyenera Kuchita: Onetsetsani kuti mwauza anthu za misonkhano yakwanu. Tchulani kuti misonkhano ndi yaulere ndiponso sayendetsapo mbale ya zopereka. Longosolani mmene misonkhano imachitikira. Auzeni kuti ndi kosi yeniyeni ya Baibulo ndipo pamakhala zophunzirira kuti onse ayendere limodzi ndi wochititsa. Auzeni za kusiyana mitundu kwa opezekapo komanso moyo wawo, ophunzira ndi osaphunzira, olemera ndi osauka. Tchulaninso kuti ofikapo ndi anthu a m’dera lomwelo ndipo ana a zaka zilizonse ndi aufulu kufikapo. Tiyenera kuitana awo amene timachita nawo phunziro, tikumawathandiza mwanjira ina iliyonse kuti afikepo.

4 Chimodzi mwa zinthu zolembedwa kumapeto m’Baibulo ndi chiitano chogwira mtima cholandira zogaŵira za Yehova zopatsa moyo chakuti: “Ndipo Mzimu ndi mkwatibwi anena, Idzani. . . . Ndipo wakumva ludzu adze; iye wofuna, atenge madzi a moyo kwaulere.” (Chiv. 22:17) Palibe chingafanane ndi kuitana ena kufika pamisonkhano yathu.

5 Mwaulosi Yesaya 60:8 amanena za zikwi mazanamazana za atamandi atsopano amene panopo akufika mumpingo wa anthu a Mulungu monga nkhunda zomwe ‘zikuuluka ngati mtambo, ndi monga nkhunda ku mazenera awo.’ Tonse tiyenera kuitanira achatsopano kumisonkhano ndi kuwalandira bwino. Mwa njira imeneyi, tidzakhala ogwirizana ndi Yehova pamene akufulumiza ntchito yosonkhanitsa.—Yes. 60:22.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena