Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • km 4/01 tsamba 1
  • “Zinthu Zonse Zitheka ndi Mulungu”

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • “Zinthu Zonse Zitheka ndi Mulungu”
  • Utumiki Wathu wa Ufumu—2001
  • Nkhani Yofanana
  • Kodi N’zosathekadi?
    Nsanja ya Olonda—2012
  • ‘Uthenga Wabwino Uwu Udzalalikidwa’
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2010
  • Pitirizanibe Kulankhula Mawu a Mulungu Mtima Molimbika
    Ogwirizana m’Kulambiridwa kwa Mulungu Yekha Wowona
  • Muzilalikira Mwakhama Ngati Yesu
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2025
Onani Zambiri
Utumiki Wathu wa Ufumu—2001
km 4/01 tsamba 1

“Zinthu Zonse Zitheka ndi Mulungu”

1 Ntchito yofunika kwambiri ya mpingo wachikristu ndiyo kulalikira uthenga wa Ufumu padziko lonse lapansi. (Mat. 24:14) Imeneyitu ndi ntchito yaikulu kwabasi. Anthu ambiri amaona kuti imafunika zinthu zambiri kuposa zimene tili nazo. Ena amaona kuti n’kosatheka kugwira ntchitoyi chifukwa anthu amatinyoza, kutitsutsa ndi kutizunza. (Mat. 24:9; 2 Tim. 3:12) Anthu osakhulupirira amaonadi kuti n’kosatheka kukwanitsa ntchitoyi. Koma, Yesu anati: “Zinthu zonse zitheka ndi Mulungu.”—Mat. 19:26.

2 Zitsanzo Zabwino Kuzitsanzira: Yesu anayamba utumiki wake ali yekhayekha pamene otsutsa anali ambiri. Adani ake pofuna kumulepheretsa ntchito yake, anam’chitira mwano m’njira zosiyanasiyana, mapeto ake anamupha imfa yopweteka kwambiri. Komabe potsiriza Yesu ananena motsimikiza kuti: “Ndalilaka dziko lapansi.” (Yoh. 16:33) Ndithudi anakwanitsa zinthu zooneka zosatheka!

3 Ophunzira a Yesu anasonyeza kulimba mtima ndi changu chofananacho mu utumiki wachikristu. Ambiri anawakwapula, kuwamenya, kuwaika mundende ngakhale kuwapha kumene. Koma “[a]nakondwera kuti anayesedwa oyenera kunyozedwa chifukwa cha dzinalo.” (Mac. 5:41) Ngakhale zinali zovuta, anakwaniritsa ntchito yooneka yosatheka, yolalikira uthenga wabwino “kufikira malekezero ake a dziko.”—Mac. 1:8; Akol. 1:23.

4 Mmene Tingakhozere Lerolino: Ifenso tikugwira ntchito yolalikira Ufumu mwachangu pamene zinthu zili zovuta kwambiri. Ngakhale pali ziletso, chizunzo, kumangidwa ndi ziwawa zina pofuna kutisiyitsa ntchitoyi, tikuitha. Kodi zikutheka bwanji? “Ndi khamu la nkhondo ayi, ndi mphamvu ayi, koma ndi Mzimu wanga, ati Yehova wa makamu.” (Zek. 4:6) Chifukwa Yehova akutilimbikitsa, palibe chingalepheretse ntchito yathu!—Aroma 8:31.

5 Polalikira, palibe chifukwa chochitira manyazi kapena mantha kapena kudziona kuti sitikuyenera. (2 Akor. 2:16, 17) Tili ndi zifukwa zazikulu zopitirizira kufalitsa uthenga wabwino wa Ufumu. Ndi thandizo la Yehova, tidzakwanitsa “zosatheka”!—Luka 18:27.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena