Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • km 8/01 tsamba 8
  • Kusangalala Kuzikhala ndi Nthaŵi Yake

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Kusangalala Kuzikhala ndi Nthaŵi Yake
  • Utumiki Wathu wa Ufumu—2001
  • Nkhani Yofanana
  • Kodi Zimene Mumachita pa Nthawi Yosangalala Zimakhala Zopindulitsa?
    Nsanja ya Olonda—2011
  • Gwiritsani Ntchito Nthawi Yanu Mwanzeru
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2005
  • Kodi Mzimu wa Dziko Ukukuipitsani?
    Nsanja ya Olonda—1997
  • Musalole Chilichonse Kusokoneza Ubwenzi Wanu ndi Yehova
    Nsanja ya Olonda—2013
Onani Zambiri
Utumiki Wathu wa Ufumu—2001
km 8/01 tsamba 8

Kusangalala Kuzikhala ndi Nthaŵi Yake

1 M’masiku ovuta ano, tonsefe timafuna kusintha zochita nthaŵi zina. Kusangalala n’kwabwino kumlingo wina wake. Komabe, kuthera nthaŵi yambiri pa zosangalatsa, maseŵera, ndiponso kucheza kungapangitse munthu kuthera nthaŵi yochepa pa zinthu zauzimu. Kusangalala kuzikhala ndi nthaŵi yake. (Mat. 5:3) Kodi izi zingachitike motani? Mwa kutsatira langizo la pa Aefeso 5:15-17.

2 Kuzikhala ndi Malire: Paulo analemba kuti Akristu afunika ‘kupenya bwino’ momwe angakhalire mwanzeru pa moyo wawo. Kusapambanitsa ndiponso kudziletsa n’kofunika kwambiri kuti tithe kuchepetsa nthaŵi yosangalala ndi kupatsa mpata zinthu zofunika kwambiri. Ndibwino kuona mofatsa momwe timagwiritsira ntchito nthaŵi yomwe timangokhala. Kusangalala kuzitithandiza m’njira zina osati kutipangitsa kuona kuti tataya nthaŵi yathu pachabe kapena kutisiya tili otopa. Ngati pambuyo pa maseŵera tikhala otopa, osasangalala, ndiponso tidzimva kuti tachimwa, n’chizindikiro chakuti tikufunika kusintha momwe timagwiritsira ntchito nthaŵi yathu.

3 Khalani Wanzeru: Paulo analangiza za ‘kuchita machawi, [“kuwombola nthaŵi,”NW]’ ya zinthu zofunika kwambiri m’moyo, osati kukhala “opusa.” Akristu odzipatulira salola moyo wawo kukhala wokondetsa zosangalatsa. Ngakhale kuti kupuma ndi kusangalala kungatipatse mphamvu, koma gwero la mphamvu yauzimu ndilo mphamvu yogwira ntchito ya Mulungu. (Yes. 40:29-31) Timalandira mzimu wake mwa kuchita zinthu za Mulungu monga kuŵerenga Baibulo, kupezeka pamisonkhano ya mpingo, kutenga mbali mu utumiki wa kumunda osati kudzera m’zosangalatsa.

4 Zinthu Zofunika Zizikhala Patsogolo: Paulo analangiza Akristu ‘kudziŵitsa chifuniro cha Ambuye n’chiyani.” Yesu anaphunzitsa kuti zochita zathu ziyenera kugona pa Ufumu wa Mulungu monga chinthu chofunika kwambiri m’moyo. (Mat. 6:33) N’kofunika kuchita kaye zinthu zimene zidzatithandiza kukhala mogwirizana ndi kudzipatulira kwathu kwa Yehova. Kenako, kusangalala kudzakhala ndi nthaŵi yake. Tikatero, kusangalala kudzakhala ndi zotsatira zabwino, ndipo tidzasangalala nako kwambiri.​—Mlal. 5:12.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena