Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • km 2/04 tsamba 1
  • Ntchito Imene Imatheka Chifukwa cha Mulungu

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Ntchito Imene Imatheka Chifukwa cha Mulungu
  • Utumiki Wathu wa Ufumu—2004
  • Nkhani Yofanana
  • Yehova Amapereka Mphamvu Yoposa Yaumunthu
    Utumiki Wathu wa Ufumu—1998
  • Muziona Mwayi Wanu wa Utumiki Monga Chinthu Chamtengo Wapatali
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2011
  • Maphunziro Ochokera kwa Mulungu Ndi Opambanadi
    Nsanja ya Olonda—2009
  • Pitirizanibe Kulankhula Mawu a Mulungu Mtima Molimbika
    Ogwirizana m’Kulambiridwa kwa Mulungu Yekha Wowona
Onani Zambiri
Utumiki Wathu wa Ufumu—2004
km 2/04 tsamba 1

Ntchito Imene Imatheka Chifukwa cha Mulungu

1 Mwa atumiki a Mulungu masiku ano, ndi ochepa amene ali ndi maphunziro apamwamba, chuma, kapena amene ali otchuka m’dzikoli. Pachifukwa chimenechi, anthu ena amangoti utumiki wathu ndi wopanda phindu. (Yes. 53:3) Komabe, ntchito imene timachitayi yophunzitsa anthu Baibulo yapatsa ambiri chitonthozo ndi chiyembekezo padziko lonse lapansi. Kodi zatheka bwanji kuti anthu wamba achite zinthu zazikulu choncho? Zatheka chifukwa cha Mulungu. (Mat. 28:19, 20; Mac. 1:8) Mtumwi Paulo anafotokoza kuti: “Zofooka za dziko lapansi Mulungu anazisankhula, kuti akachititse manyazi zamphamvu.”—1 Akor. 1:26-29.

2 Atumwi ambiri komanso Akristu ena a m’zaka 100 zoyambirira za nyengo yathu ino anali “osaphunzira ndi opulukira [“anthu wamba,” NW].” (Mac. 4:13) Ngakhale ndi choncho, iwo molimba mtima anachita ntchito yawo yolalikira uthenga wabwino, ndipo Yehova anawadalitsa. Ngakhale kuti iwo anakumana ndi mavuto ndi anthu otsutsa, “mawu a Ambuye anachuluka mwamphamvu nalakika.” Palibe chimene chikanaletsa ntchitoyo chifukwa Mulungu ndiye anali mwiniwake. (Mac. 5:38, 39; 19:20) Ndi mmenenso zilili masiku ano. Ngakhale olamulira amphamvu amene ayesetsa kutsutsa kuti uthenga wabwino usachuluke ndi kulakika alephera.—Yes. 54:17.

3 Ulemu Wonse Upite kwa Mulungu: Kodi mwayi umene tili nawo wokhala atumiki a Mulungu umatipatsa chifukwa chodzitamandira? Kutalitali. Za utumiki wachikristu, Paulo analemba kuti: “Tili nacho chuma ichi m’zotengera zadothi, kuti ukulu woposa wamphamvu ukhale wa Mulungu, wosachokera kwa ife.” (2 Akor. 4:7) Paulo anazindikira kuti anatha kuchita utumiki wake chifukwa cha nyonga imene Mulungu anam’patsa.—Aef. 6:19, 20; Afil. 4:13.

4 Ifenso timazindikira kuti ntchito yathu yolalikira ikutheka chifukwa ‘chothandizidwa ndi Mulungu.’ (Mac. 26:22) Mwa ntchito yolengeza imeneyi padziko lonse, Yehova akutigwiritsa ntchito mwamphamvu kugwedeza amitundu monga chizindikiro cha chiwonongeko choopsa chimene chikudza posachedwa. (Hag. 2:7) Komatu ndiye tili ndi mwayi waukulu pokhala “antchito anzake a Mulungu” pantchito yaikuluyi yotuta mwauzimu!—1 Akor. 3:6-9.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena