Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • km 6/04 tsamba 8
  • Zomwe Munganene Pogaŵira Magazini

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Zomwe Munganene Pogaŵira Magazini
  • Utumiki Wathu wa Ufumu—2004
  • Nkhani Yofanana
  • Zomwe Munganene Pogaŵira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2004
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2006
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2008
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2010
Onani Zambiri
Utumiki Wathu wa Ufumu—2004
km 6/04 tsamba 8

Zomwe Munganene Pogaŵira Magazini

Nsanja ya Olonda June 15

“Kodi mukuganiza bwanji, kuphunzitsa ana masiku ano n’kovuta kapena ayi? [Yembekezani ayankhe.] Taonani mfundo iyi yotsimikizira kuti makolo angakwanitse kuchita zimenezo. [Ŵerengani Miyambo 22:6.] Nsanja ya Olonda iyi ili ndi malangizo abwino othandiza makolo kuti akwanitse ntchito yovuta imeneyi.”

Galamukani! July 8

“Anthu ena amaganiza kuti kukhulupirira Mulungu sikugwirizana ndi sayansi. Koma kodi mukudziŵa kuti pali akatswiri a sayansi amene amanena kuti sayansi imalimbikitsa chikhulupiriro choti kuli Mlengi? [Yembekezani ayankhe.] Galamukani! iyi ikufotokoza maumboni ena amene achititsa asayansiŵa kunena zimenezi.” Ŵerengani Aroma 1:20.

Nsanja ya Olonda July 1

“Panthaŵi za mavuto, anthu ambiri amakayika ngati Mulungu amaganiziradi anthu ndiponso ngati amaona kuvutika kwawo. Kodi inunso munakayikirapo? [Yembekezani ayankhe.] Magazini iyi ikufotokoza mmene Mulungu amasonyezera kuti amatiganizira masiku ano ndi mmene waperekera njira yothetsera kuvutika konse.” Ŵerengani Yohane 3:16.

Galamukani! July 8

“Kwa anthu ambiri, unyamata ndi nthaŵi yosangalatsa komanso yovuta, kodi simukuvomereza zimenezi? [Yembekezani ayankhe.] Magazini ino ikufotokoza kusintha kumene kumachitika pa unyamata. Ikufotokozanso malangizo anzeru amene angathandize achinyamata ameneŵa kugwiritsa ntchito bwino unyamata wawo.” Ŵerengani Mlaliki 12:1.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena