Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • km 5/04 tsamba 4
  • Zomwe Munganene Pogaŵira Magazini

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Zomwe Munganene Pogaŵira Magazini
  • Utumiki Wathu wa Ufumu—2004
  • Nkhani Yofanana
  • Zomwe Munganene Pogaŵira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2004
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2006
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2007
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2009
Onani Zambiri
Utumiki Wathu wa Ufumu—2004
km 5/04 tsamba 4

Zomwe Munganene Pogaŵira Magazini

Nsanja ya Olonda May 15

“Kodi munayamba mwalingalirapo ngati zinthu zimene anthu amachita padziko pano zimam’khudza Mulungu? [Yembekezani ayankhe.] Onani mmene zochita zathu zingakhudzire mtima wa Mulungu. [Ŵerengani Miyambo 27:11.] Magazini iyi ikufotokoza zitsanzo zina za anthu amene anakondweretsa mtima wa Mulungu, ndipo ikufotokoza mmene ifeyo tingachitire zomwezo.”

Galamukani! June 8

“Sayansi ya zamankhwala yapita patsogolo zedi polimbana ndi matenda, koma kodi mukuganiza kuti tidzakhala ndi dziko lopanda matenda alionse? [Yembekezani ayankhe.] Magazini iyi ikufotokoza kuti tsiku lina aliyense padziko lapansi adzakhala ndi thanzi langwiro pokwaniritsa lonjezo ili.” Ŵerengani Yesaya 33:24.

Nsanja ya Olonda June 1

“Anthu ena amaona kuti sikofunika kukhala m’chipembedzo chinachake pofuna kulambira Mulungu. Kodi munayamba mwaganizapo zimenezi? [Yembekezani ayankhe.] Magazini iyi ikufotokoza mbiri ya zochita za Mulungu ndi anthu m’nthaŵi zakale. Ikufotokozanso zimene kulambira Mulungu m’choonadi kumatanthauza.” Ŵerengani Yohane 4:24.

Galamukani! June 8

“Anthu ambiri masiku ano amasungulumwa. Zimenezi zimaphatikizapo kuona kuti anthu sakukufuna. Kodi simukuvomereza kuti zimenezi zingakhale zopweteka? [Yembekezani ayankhe. Ndiyeno ŵerengani Salmo 25:16.] Magazini iyi ya Galamukani! ikupereka mfundo zothandiza zogonjetsera kusungulumwa.”

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena